Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Tsiku lamene ndinanyamukila panyumba kuyenda kumzinda El día que dejé mi casa para irme a la ciudad

Texto Lesley Koyi, Ursula Nafula

Ilustraciones Brian Wambi

Translated by Jones Jere Joshua

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 3

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Poimilila mabasi ag’ono kumudzi kwathu panali potangwanidwa ndi mabasi olonga kwambili. Pansi panalinso katundu oculuka ofunika kulongedwa. Oitanitsa anthu anali kufuula maina akumene mabasi amapita.

La pequeña parada de autobuses de mi aldea estaba llena de gente y de autobuses sobrecargados. En el suelo había aun más cosas por cargar. Los pregoneros anunciaban los lugares a los que iban sus autobuses.


“Tauni! Tauni! Kupita kumadzulo!” Ndinamvela oitanitsa kufuula. Iyo ndiyo basi ndimafuna kukwela.

“¡A la ciudad! ¡A la ciudad! ¡Autobús hacia el oeste!” escuché que gritaba un pregonero. Ése era el autobús que yo necesitaba tomar.


Basi yakutauni inali pafupi kudzala, koma anthu ambili anali akali kukankha kuti alowe. Ena analonga katundu yao munsi mwa basi. Ena anaika moika katundu mkati mwa basi.

Aunque el autobús con destino a la ciudad estaba casi lleno, había más gente empujando para subirse. Algunos ponían su equipaje en la parte de abajo. Otros lo ponían en las repisas de adentro.


Okwela atsopano anagwila matikiti ao pomwe amafuna-funa pomwe angakhale mu basi yodzala ndi anthu. Azimai a ana ang’ono ang’ono anawakhazika bwino paulendo utali.

Los pasajeros recién llegados se subían al autobús con sus boletos en mano buscando un asiento. Las mujeres con hijos pequeños los confortaban para el largo viaje.


Ndinaziika pafupi ndi dzenela. Munthu amena anakhala pafupi ndi ine anagwilila pulasitiki ya msipu. Anavala nkhwawilo zakale, khoti lakutha, ndipo amaoneka wamantha.

Me apretujé al lado de una ventana. La persona a mi lado sujetaba con fuerza una bolsa de plástico verde. Llevaba sandalias viejas, un abrigo harapiento, y se veía nervioso.


Ndinapenya kubwalo kwa basi ndipo ndinazindikila kuti ndinali kusiya mudzi wanga, kumalo komwe ndinakulila. Ndinali kupita ku tauni yaikulu.

Miré por la ventana del autobús y me di cuenta de que estaba dejando atrás mi aldea, el lugar donde había crecido. Ahora me iba a la gran ciudad.


Kulonga kunamalizika ndipo aulendo onse anakhazikika pansi. Azamalonda naonso anali kuzipatikiza kulowa mubasi kugulitsa katundu wao ku aulendo. Aliyense anali kufuula maina azomwe zinalipo zogulitsa. Mau anamveka odabwitsa kwa ine.

Terminaron de cargar el autobús y todos los pasajeros se sentaron. Los vendedores ambulantes se apretujaron para entrar a venderle sus productos a los pasajeros. Gritaban los nombres de lo que tenían para vender. Las palabras me parecían graciosas.


Aulendo ang’ono anagulako zakumwa, ena anagulako zakudya zotsekemela za zing’ono zing’ono ndipo anayamba kutamfuna. Aja amene analibe ndalama, monga ine tinangopenyelela.

Algunos pasajeros compraron bebidas, otros compraron pequeños refrigerios y empezaron a comer. Los que no tenían dinero, como yo, solamente nos quedamos mirando.


Zocita zimenezi zinasokonezedwa ndi kulila kwa huta ya bus, kudziwitsa kuti tinali pafupi kunyamuka. Onenezela anafuulila ogulitsa kuti atuluke kubwalo.

Todo este ajetreo fue interrumpido por el claxon del autobús, señal de que estábamos listos para partir. El pregonero gritó a los vendedores ambulantes para que se bajaran.


Ogulitsa anakankhana wina ndi mnzace kuti atuluke mu basi. Ena anali kupeleka chenji kwa apaulendo. Ena amayesa kugulitsa zinthu zao nthawi yothela.

Los vendedores ambulantes se empujaban para salir del autobús. Algunos le entregaron su cambio a los pasajeros. Otros intentaron vender productos por última vez.


Pomwe basi imacoka pa sitesheni ya basi, ndinayangana padzenela. Ndinaganizila ngati ndizabwelanso kumudzi wanga.

Mientras el autobús partía desde la estación, miré por la ventana. Me preguntaba si alguna vez volvería a mi aldea.


Pomwe ulendo umacitika, mkati mwa basi munatentha kwambili. Ndinatseka maso anga kuyesa kugona.

A medida que pasaba el tiempo, el autobús se puso muy caluroso. Cerré los ojos con la esperanza de quedarme dormido.


Koma maganizo anabwelelanso kumudzi. Kodi amai anga adzakhala bwino? Kodi akalulu anga azabweletsa ndalama zilizonse? Kodi mukulu wanga adzakumbukila kuthilila mbeu zanga zamitengo?

Pero volví a pensar en mi casa. ¿Estará a salvo mi madre? ¿Traerán dinero mis conejos? ¿Se acordará mi hermano de regar los árboles que planté?


Mnjila, ndinakumbukila dzina ya malo amene amalume anakhalako mu mzinda ukulu. Ndinali ndikali kung’ung’udzila pamene tulo tunanigwila ndipo ndinagona.

Mientras viajaba, recitaba el nombre del lugar donde vivía mi tío en la gran ciudad. Seguí murmurando ese nombre mientras dormía.


Maola asanu ndi anai atsatila, ndinauka ndi phokoso lalikulu ndi kuitana kwa apaulendo amubasi apita kumudzi kwanga. Ndinatenga cola canga cacing’ono ndi kulumphila kubwalo kwa basi.

Nueve horas más tarde, desperté escuchando fuertes golpeteos y gritos llamando a los pasajeros que viajaban de vuelta a mi aldea. Tomé mi pequeño morral y me bajé del autobús.


Basi yobwelela kumudzi imadzala mofulumila. Mosacedwa inayamba ulendo wopita kum’mawa. Cofunikila ceni-ceni kwa ine tsopano, cinali cakuyamba kufuna-funa nyumba ya amalume anga.

El autobús de vuelta a mi aldea se llenó rápidamente. Pronto empezaría su viaje de vuelta al este. Por ahora, lo más importante para mí era empezar a buscar la casa de mi tío.


Texto: Lesley Koyi, Ursula Nafula
Ilustraciones: Brian Wambi
Translated by: Jones Jere Joshua
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 3
Fuente: The day I left home for the city del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 4.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF