Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Mwana wa Bulu El Niño Burro

Texto Lindiwe Matshikiza

Ilustraciones Meghan Judge

Translated by David Sani Mwanza

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 3

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Kanali kamwana kakakazi kang’ono komwe kanaona chinthu cha maonekedwe odabwisa patali.

Una niña pequeña fue la primera en ver una figura misteriosa a lo lejos.


Pamane chinthu chinabwela pafupi, anaona kuti anali mzimai ome anali ndi mimba yaikulu.

Mientras la figura se acercaba, la niña se dio cuenta que era una mujer embarazada a punto de dar a luz.


Mwamanyazi koma mopanda mantha, kamwana kayenda pafupi ndi mzimai. “Tifunika kukhala nao pamozi,” anthu a kamwana kakazi anavomekezana. “Tizamusunga ndi mwana wake bwino-bwino.

Tímida pero valientemente, la pequeña niña se acercó a la mujer. “Tenemos que cuidar de ella,” decidieron los familiares de la niña pequeña. “Ella y su bebé estarán a salvo con nosotros”.


Mwana anali pafupi kubadwa. “Kankha!” “Bwelesani zovimba!” “Water!” “Kankhaaaa!!!”

Al poco tiempo, el bebé empezó a nacer. “¡Puja!” “¡Traigan mantas!” “¡Agua!” “¡¡¡Puuuuujjjjjaaa!!!”


Koma pamene anaona mwana wakhanda, aliyense anabwelera m’mbuyo ndi kudabwa. “Bulu?!”

Pero cuando vieron al recién nacido, todos se llevaron una gran sorpresa. “¡¿Un burro?!”


Aliyense anayamba kukangana. “Tinakamba kuti tizamusunga pamozi ndi mwana wake bwino-bwino, ndipo tizachita motero,” ena anatero. “Koma azatibweretsera soka!” enanso ananena.

Todos empezaron a discutir. “Prometimos que cuidaríamos de la madre y su hijo, y eso es lo que haremos,” decían algunos. “¡Pero ellos nos van a traer mala suerte!” decían otros.


Chifukwa cha icho, mzimai anasala yekha. Anavutika kuganiza zomwe azachita ndi mwana wodabwisa. Anavutika kuganiza kuti azazichita chani.

Y así fue como la madre volvió a quedar sola otra vez. Se preguntaba qué hacer con este extraño bebé. Se preguntaba qué hacer consigo misma.


Koma pothera, anafunika kuvomela kuti bulu anali mwana wake ndipo anali mai wake.

Pero finalmente tuvo que aceptar que ese era su bebé y que ella era su madre.


Tsono, ngati mwana anakhala chimozimozi, ndi thupi ing’ono, zinthu zinakakhalako bwino. Koma bulu anakula ndi kukula kufikila nthawi yomwe sankakhala pa mbuyo pa mai wake. Ndipo mukhalidwe wake unasiyana ndi munthu. Amai ake anli olema nthawi zambili komanso aukali. Nthawi zina, anatuma mwana kuchita nchito zomwe zinafunikila kuchitika ndi nyama.

Si el niño se hubiera quedado del mismo tamaño, todo habría sido diferente. Pero el niño burro creció y creció hasta que su madre no pudo cargarlo más en su espalda. Y no importaba cuánto lo intentase, el niño burro no lograba comportarse como un niño humano. Su madre se la pasaba cansada y frustrada. A veces ella le ordenaba hacer trabajo de animales.


Msokonezo ndi mkwiyo unakula mu mtima wa bulu. Anali kulephela kuchita zilizonse. Analephela kukhali ndi mkhalidwe weni weni. Anali okwiya kotelo kuti, tsiku lina, anamenyesela amai ake pansi.

Burro sentía cada vez más confusión y rabia. Que no podía hacer esto, que no podía hacer aquello. Que él no podía ser esto ni aquello. Un día se puso tan furioso que botó a su madre al suelo de una patada.


Bulu anachita manyazi. Anayamba kuthawila kutali komwe angathe kupita.

Burro se sintió lleno de vergüenza. Corrió tan rápido y lejos como pudo.


Pa nthawi yamene analeka kuthawa, unali usiku, Bulu anasowa. “Hee, hyu?” anatelo ku mdima. Anafika pamathelo. Anayamba kusanduka. Anagona mu tulo twatukulu twa mavuto.

Cuando dejó de correr, ya era de noche y Burro estaba perdido. “¿Hiaaa?” susurró en la oscuridad. “¿Hiaaa?” le respondió su eco. Estaba solo. Se acurrucó y cayó rendido en un sueño profundo e intranquilo.


Bulu anauka ndi kupeza nkhalamba ili kumuyangana. Anayangana mu maso a mdala ndi kuyamba kukhala ndi chiyembekezo.

Cuando Burro despertó, había un extraño anciano mirándolo. Burro le miró a los ojos y comenzó a sentir una chispa de esperanza.


Bulu afuna kukhala ndi mdala, omwe anamuphunzisa njira zambili zomwe angakhalilemo umoyo. Bulu anamva ndi kuphunzila, chimozi mozi mdala nayenso anamvesera ndi kuphunzila. Anathandizana ndipo anaseka pamozi.

Burro se fue a vivir con el anciano, quien le enseñó muchas formas diferentes de sobrevivir. Burro escuchaba y aprendía, y lo mismo hacía el anciano. Se ayudaban y reían juntos.


Tssiku lina m’mawa, mdala anapempha Bulu kuti amunyamule kumupeleka pa mwamba pa phiri.

Una mañana, el anciano le pidió a Burro que lo llevara hasta la cima de una montaña.


Pamwamba pa mithambo, anagona. Bulu analota kuti amai ake anli kudwala ndipo anali kumuitana. Ndipo pamene anauka…

Se quedaron dormidos más arriba de las nubes. Burro soñó que su madre estaba enferma y que lo llamaba. Y cuando despertó…


Mithambo inachoka pamozi ndi mzake, mdala.

…las nubes habían desaparecido junto con su amigo, el anciano.


Bulu anaziwa zomwe anafunika kuchita.

Burro finalmente se dio cuenta de lo que tenía que hacer.


Buu anapeza amai ake, okha ali kulilila mwana wao wosowa. Anapenyana kwakanthawi, ndipo anakumbatilana mwamphamvu.

Burro encontró a su madre, sola y llorando por su hijo perdido. Se quedaron mirándose a los ojos por largo tiempo. Luego se abrazaron muy apretadamente.


Bulu ndi amai ake akulila pamozi ndi anapeza nzila zosiyanasiyana zokhalilamo pamozi. Pang’ono pang’ono, onse anthu okhala pafupi nao ndi banja lao ayamba kukhala nao pamozi mopanda vuto lenileni.

El hijo burro y su madre ya llevan tiempo creciendo juntos y han aprendido a convivir. Lentamente, otras familias se han instalado a vivir cerca de ellos.


Texto: Lindiwe Matshikiza
Ilustraciones: Meghan Judge
Translated by: David Sani Mwanza
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 3
Fuente: Donkey Child del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 4.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF