Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Anansi ndi Nzelu Anansi y la sabiduría

Texto Ghanaian folktale

Ilustraciones Wiehan de Jager

Translated by Sitwe Benson Mkandawire

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 3

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Matsiku amakedzana, anthu sanali kudziwa ciliconse. Sanadziwe kubzala mbeu, mwina kusoka zovala, mwina kupanga zisulo kucoka kunsimbi. Mulungu ochedwa Nyame wakumwamba anali ndi nzelu pa zonse zamziko. Nzeluzi anazisungilira bwinobwino mu poto yopangidwa ndi dothi.

Hace mucho, mucho tiempo la gente no sabía nada. No sabían cómo cultivar, o cómo tejer tela, o cómo hacer herramientas de hierro. El dios Nyame arriba en el cielo tenía toda la sabiduría del mundo. La mantenía guardada en una vasija de barro.


Tsiku lina, Nyame anaganiza kupatsa Anansi poto ya nzelu. Nthawi iliyonse Anansi anayangana mupoto, anaphunziramo cinthu cimodzi catsopano. Anali okondwera kwambiri.

Un día, Nyame decidió darle la vasija de sabiduría a Anansi. Cada vez que Anansi se asomaba y miraba dentro de la vasija de barro, aprendía algo nuevo. ¡Qué impresionante!


Maganizo a utani anabwera muli Anansi, “Poto yanzelu ndizaisugilira bwinobwino pamwamba pa mtengo. Mwakuti inde ndekha ndikhale ndi nzelu!” Anatenga nthambo itali nakumangilira poto pamala. Anayamba kukwela mtengo. Koma cinali covuta kukwela cifukwa poto inali kumukhumya kumyendo nthawi yonse.

El codicioso Anansi pensó, “voy a guardar la vasija en la copa de un árbol muy alto. ¡Y será sólo mía!” Hiló un hilo largo, envolvió con él la vasija de barro, y lo ató a su cintura. Empezó a trepar el árbol. Pero se le hacía muy difícil trepar el árbol con la vasija constantemente pegándole en las rodillas.


Pamene zonsezi zinali kucitika, mwana mwamuna mung’ono wa Anansi anali kutamba pansi pacimtengo imilire. Iye anati, “Kodi sicizakhala capafupi kukwela mtengo ngati mwamangilira poto kumusana?” Anansi anayesa kumangilira poto ya nzelu kumusana ndipo iye anakwela mtengo kosavutika.

Mientras tanto, el hijo pequeño de Anansi lo miraba desde abajo y le dijo, “¿No sería más fácil trepar si te ataras la vasija a tu espalda?” Anansi ató la vasija llena de sabiduría a su espalda y, efectivamente, fue mucho más fácil.


Posacedwa anafike pamwamba pa mtengo. Koma iye anaganiza, “Ine ndine nifunikira kukhala ndi nzelu zonse, koma apa mwana wanga ndiye anali na nzelu kucila ine!” Anansi anakalipa kwambiri paizi ndiponso, anataya poto ya nzelu pansi kucoka mucimtengo.

En un instante logró llegar a la copa del árbol. Pero entonces se detuvo a pensar: “Se supone que yo soy quien tiene toda la sabiduría, ¡pero mi hijo fue más listo que yo!” Anansi se enojó tanto que lanzó la vasija desde lo alto del árbol.


Poto yanzelu inang’ambika mutuzidunswa pamene inafika pansi. Nzelu zinafarisidwa ku munthu aliyonse. Ndiye mwamene anthu anaphunzilira kulima, kusoka zovala, kupanga zisulo za nsimba ndi zinthu zina zamene anthu aziwa kucita.

Quedó hecha pedazos en el suelo. La sabiduría quedó libre y disponible para todos. Y así fue cómo la gente supo cultivar, tejer, hacer herramientas de hierro, y muchas otras cosas más.


Texto: Ghanaian folktale
Ilustraciones: Wiehan de Jager
Translated by: Sitwe Benson Mkandawire
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 3
Fuente: Anansi and Wisdom del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 3.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF