Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Kambewu: Nkhani ya Wangari Maathai Una pequeña semilla: la historia de Wangari Maathai

Texto Nicola Rijsdijk

Ilustraciones Maya Marshak

Translated by Gridon Mwale

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 3

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Pamudzi wina womangidwa pamatero ya phiri la Kenya kumwawa kwa Africa, Kunali kamtsikana kena dzina lake Wangari. Wangari ndi amai ake anali kugwira ntchito zaminda.

En una aldea ubicada en la cuesta del Monte Kenia en África del Este, una niña pequeña trabajaba en los campos con su madre. Su nombre era Wangari.


Wangari anali mtsikana wokonda kucezera pabwalo. Tisku lina Wangari anagaula mudimba mwao nabzyala tumbewu pansi pomwe panali potentha kwambiri.

A Wangari le encantaba estar afuera. En el huerto de su familia, ella separaba la tierra con su machete y plantaba pequeñas semillas en la tierra tibia.


Thawi imene anali kukonda kwambiri mtsikanayu tsiku lililonse inali pamene dzuwa litangolowa kumene. Ndipo mudima ukagwira chakuti zomera zamthengo zaleka kuoneka, Wangari anali kudziwa kuti thawi yopita ku nyumba yafika tsopano. Ndipo popita kunyumba anali kudzera njira zang’ombe, kuwoloka mitsinje ndi kudutsa minda mpaka kufika kwao.

Su momento favorito del día era justo después del anochecer. Cuando se ponía muy oscuro y no podía mirar las plantas. Entonces era cuando Wangari sabía que debía regresar a casa. Ella caminaba por los senderos angostos del campo, cruzando los ríos que estaban en su camino.


Wangari anali mwana wocenjera kwambiri ndipo anali wofunitsitsa kupita kusukulu kukaphunzira. Koma makolo ake sanafune kuti kamtsikana aka kaphunzire koma kazikhala pa nyumba ndi kugwira ncthito. Pamene Wangari anali ndi zaka 7, mukulu wake wamwamuna anagonjetsa makolo awo pokambirana kuti Wangari apite kusukulu akaphunzire.

Wangari era una niña astuta y no podía esperar para ir a la escuela. Pero su madre y padre querían que ella se quedara para ayudarlos con los quehaceres del hogar. Cuando cumplió siete años, su hermano mayor convenció a sus padres para que ella fuera a la escuela.


Wangaari anakonda kuphunzira kwambir chotero kuti anaphunzira kopitirira kupyolera mkuwerenga mabuku osiyanasiyana. Ndipo anakhoza kwambiri pa sukulu chotero kuti anapeza umwayi wokaphunzira ku dziko lakutali la United States of America. Wangari anasangalala kwambiri chifukwa anali kufunitsitsa kudziwa zambiri zapa dziko lapansi.

¡A ella le gusta aprender! Wangari aprende muy rápido con cada libro que lee. A ella le iba tan bien en la escuela que la invitaron a estudiar en Estados Unidos. ¡Wangari estaba muy entusiasmada! Ella quería aprender más acerca del mundo.


Wangari anaphunzira zinthu zambiri pamene anali pa American Univeziti. Anaphunzira pa zomera ndi mumene zimakulira. Zimenezi zinamukumbutsa mumene anali kusewerera ndi abale ake mthunzi ya mitengo mthengo laku-dziko lokongola la Kenya.

En la universidad americana, Wangari aprendió muchas cosas nuevas. Ella estudió sobre las plantas y cómo ellas crecen. Y recordó cómo ella creció: jugando con su hermano bajo la sombra de árboles hermosos en los bosques de Kenia.


Pamene anali kuphunzira tsiku ndi tsiku anazindikira kuti akonda anthu akwao ku Kenya. Anali kufuna kuti anthu kudziko limeneli tsiku lina akapate ufulu ndi mtendere. Ndipo anayewa dziko lakwao pamene anapitiliza ndi maphunziro. ake kwakanthawi.

Mientras más aprendía, más se daba cuenta de que le encantaba la gente de Kenia. Ella quería que ellos fueran felices y libres. Mientras más aprendía, más recordaba su casa en África.


Anabwerera kudziko lakwao ku Kenya pamane anamaliza maphunziro ake ndipo nthawi imeneyi dziko la Kenya linali litasintha. Mapulazi akuluakulu anatenga malo ochuluka. Azimai anali kusowa kotheba nkhuni chifukwa mitengo kunalibe. Anthu anali osauka ndipo ana anali kuoneka anjala.

Al finalizar sus estudios, regresó a Kenia. Pero su país había cambiado. Habían granjas enormes que atravesaban todo el territorio. Las mujeres no tenían madera para hacer fogatas para cocinar. La gente era pobre y los niños tenían hambre.


Wangari anali kudziwa chofunika kuchita kuti athetsa mabvuto amenewa: anaphunzitsa azimai kubzyala mitengo kuchokera kumbewu. Azimai amenewa anayamba kugulitsa mitengo zao zitakula ndikupeza ndalama zosamalira ma banja awo. Chifukwa cacimenechi azimai anakhala wokondwera kwambiri ndi Wangari amene anawa thandiza kuti akhale ndi mphanvu komanso olimba.

Wangari sabía qué hacer. Les enseñó a las mujeres a plantar árboles con semillas. Las mujeres vendían los árboles y usaban aquel dinero para cuidar a sus familias. Las mujeres estaban muy contentas. Wangari las había ayudado a sentirse poderosas y fuertes.


Patapita zaka zambiri, mitengo zimene zinabzyalidwa zija, zinakula ndi ku panga thengo. Mitsinje inayambanso kukhala ndi madzi. Mbiri ya Wangari inafika ponseponse mu Africa. Lerolino, mitengo zamitundumitundu mamilyoni tilikuonazi zinachokera ku mbewu ya Wangari.

Con el paso del tiempo, los árboles nuevos siguieron creciendo hacia el bosque, y los ríos comenzaron a fluir nuevamente. El mensaje de Wangari se difundió por toda África. Hoy en día, millones de árboles han crecido gracias a las semillas de Wangari.


Wangari anasewenzadi mwamphanvu. Chotero kuti anthu dziko lonse lapnansi anazindikila ntchito yaikula yomwe anacita, ndipo ana patsidwa mphoto yodziwika kwambiri padziko lonse lapansi. Mphoto imeneyi inali kutchedwa kuti Kulemekezedwa ndi Mtendere, ndipo anakhala mkazi woyamba mu Africa kulandila mphoto yotero.

Wangari había trabajado muy duro. La gente de alrededor del mundo lo notó, y le otorgaron un premio famoso. Se llama Premio Nobel de la Paz ella fue la primera mujer africana en recibirlo.


Wangari anamwalira mu caka ca 2011, koma timamukumbukila tikamaona mtengo wokongola uliwonse mthengo.

Wangari murió el año 2011, pero la podemos recordar cada vez que miramos un hermoso árbol.


Texto: Nicola Rijsdijk
Ilustraciones: Maya Marshak
Translated by: Gridon Mwale
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 3
Fuente: A Tiny Seed: The Story of Wangari Maathai del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 4.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF