Le petit arrêt d’autobus dans mon village était occupé par des tas de gens et des autobus surchargés. Sur le sol il y avait encore plus de choses à charger. Les revendeurs de billets criaient les noms des endroits où leurs autobus allaient.
“Tauni! Tauni! Kupita kumadzulo!” Ndinamvela oitanitsa kufuula. Iyo ndiyo basi ndimafuna kukwela.
J’entendis un revendeur de billets crier: « Ville ! Ville ! Direction ouest ! ». C’était l’autobus que je devais prendre.
Basi yakutauni inali pafupi kudzala, koma anthu ambili anali akali kukankha kuti alowe. Ena analonga katundu yao munsi mwa basi. Ena anaika moika katundu mkati mwa basi.
L’autobus de ville était presque plein, mais plus de personnes poussaient encore pour embarquer. Quelques-unes chargèrent leurs valises sous l’autobus. D’autres mirent les leurs sur les étagères à l’intérieur.
Okwela atsopano anagwila matikiti ao pomwe amafuna-funa pomwe angakhale mu basi yodzala ndi anthu. Azimai a ana ang’ono ang’ono anawakhazika bwino paulendo utali.
Des nouveaux passagers agrippaient leurs billets tandis qu’ils cherchaient un endroit pour s’asseoir dans l’autobus. Des femmes avec de jeunes enfants les installaient confortablement pour le long voyage.
Ndinaziika pafupi ndi dzenela. Munthu amena anakhala pafupi ndi ine anagwilila pulasitiki ya msipu. Anavala nkhwawilo zakale, khoti lakutha, ndipo amaoneka wamantha.
Je me suis serré à côté d’une fenêtre. La personne à côté de moi tenait un sac vert en plastique fermement. Il portait de vieilles sandales, un manteau usé, et il semblait nerveux.
Ndinapenya kubwalo kwa basi ndipo ndinazindikila kuti ndinali kusiya mudzi wanga, kumalo komwe ndinakulila. Ndinali kupita ku tauni yaikulu.
Je regardai à l’extérieur de l’autobus et je réalisai que je quittais mon village, l’endroit où j’avais grandi. Je me rendais à la grande ville.
Kulonga kunamalizika ndipo aulendo onse anakhazikika pansi. Azamalonda naonso anali kuzipatikiza kulowa mubasi kugulitsa katundu wao ku aulendo. Aliyense anali kufuula maina azomwe zinalipo zogulitsa. Mau anamveka odabwitsa kwa ine.
Le chargement était complet et tous les passagers étaient assis. Des colporteurs se frayaient encore un passage dans l’autobus pour vendre leurs marchandises aux passagers. Chacun criait les noms des articles disponibles. Les mots me semblaient drôles.
Aulendo ang’ono anagulako zakumwa, ena anagulako zakudya zotsekemela za zing’ono zing’ono ndipo anayamba kutamfuna. Aja amene analibe ndalama, monga ine tinangopenyelela.
Quelques passagers achetèrent des breuvages, d’autres achetèrent des petites collations et commencèrent à manger. Ceux qui n’avaient pas d’argent, comme moi, observaient seulement.
Zocita zimenezi zinasokonezedwa ndi kulila kwa huta ya bus, kudziwitsa kuti tinali pafupi kunyamuka. Onenezela anafuulila ogulitsa kuti atuluke kubwalo.
Ces activités furent interrompues par le klaxonnement de l’autobus, un signe que nous étions prêts à partir. Le revendeur de billets cria aux colporteurs de sortir.
Ogulitsa anakankhana wina ndi mnzace kuti atuluke mu basi. Ena anali kupeleka chenji kwa apaulendo. Ena amayesa kugulitsa zinthu zao nthawi yothela.
Les colporteurs se poussaient pour sortir de l’autobus. Quelques-uns ont redonné de la monnaie au voyageurs. D’autres ont fait des tentatives de dernière minute pour vendre d’autres articles.
Pomwe basi imacoka pa sitesheni ya basi, ndinayangana padzenela. Ndinaganizila ngati ndizabwelanso kumudzi wanga.
Lorsque l’autobus quitta l’arrêt, j’ai regardé par la fenêtre fixement. Je me demandais si je retournerais à mon village un jour.
Pomwe ulendo umacitika, mkati mwa basi munatentha kwambili. Ndinatseka maso anga kuyesa kugona.
Alors que le voyage avançait, l’intérieur de l’autobus est devenu très chaud. J’ai fermé les yeux en espérant dormir.
Mais je repensais toujours à chez moi. Est-ce que ma mère serait en sécurité ? Est-ce que mes lapins rapporteraient de l’argent ? Est-ce que mon frère se souviendrait d’arroser mes semis d’arbres ?
Mnjila, ndinakumbukila dzina ya malo amene amalume anakhalako mu mzinda ukulu. Ndinali ndikali kung’ung’udzila pamene tulo tunanigwila ndipo ndinagona.
En chemin, j’ai mémorisé le nom de l’endroit où mon oncle vivait dans la grande ville. Je le marmonnais encore lorsque je me suis endormi.
Maola asanu ndi anai atsatila, ndinauka ndi phokoso lalikulu ndi kuitana kwa apaulendo amubasi apita kumudzi kwanga. Ndinatenga cola canga cacing’ono ndi kulumphila kubwalo kwa basi.
Neuf heures plus tard, je me suis réveillé au bruit de quelqu’un qui appelait les passagers qui retournaient au village. J’ai ramassé mon petit sac et j’ai sauté de l’autobus.
Basi yobwelela kumudzi imadzala mofulumila. Mosacedwa inayamba ulendo wopita kum’mawa. Cofunikila ceni-ceni kwa ine tsopano, cinali cakuyamba kufuna-funa nyumba ya amalume anga.
L’autobus de retour se remplissait rapidement. Bientôt il partirait vers l’est. La chose la plus importante pour moi maintenant était de commencer à chercher la maison de mon oncle.