Téléchargement PDF
Retour à la liste des contes

Kambewu: Nkhani ya Wangari Maathai Une petite graine : l'histoire de Wangari Maathai

Écrit par Nicola Rijsdijk

Illustré par Maya Marshak

Traduit par Gridon Mwale

Lu par Christine Mwanza

Langue chewa

Niveau Niveau 3

Lire l’histoire en entier L’enregistrement audio de cette histoire est actuellement indisponible.


Pamudzi wina womangidwa pamatero ya phiri la Kenya kumwawa kwa Africa, Kunali kamtsikana kena dzina lake Wangari. Wangari ndi amai ake anali kugwira ntchito zaminda.

Dans un village situé sur les flancs du Mont Kenya en Afrique de l’Est, une petite fille travaillait dans les champs avec sa mère. Son nom était Wangari.


Wangari anali mtsikana wokonda kucezera pabwalo. Tisku lina Wangari anagaula mudimba mwao nabzyala tumbewu pansi pomwe panali potentha kwambiri.

Wangari aimait beaucoup être dehors. Dans le potager de sa famille, elle faisait des trous dans le sol avec sa machette. Elle enfouissait des petites graines dans la terre chaude.


Thawi imene anali kukonda kwambiri mtsikanayu tsiku lililonse inali pamene dzuwa litangolowa kumene. Ndipo mudima ukagwira chakuti zomera zamthengo zaleka kuoneka, Wangari anali kudziwa kuti thawi yopita ku nyumba yafika tsopano. Ndipo popita kunyumba anali kudzera njira zang’ombe, kuwoloka mitsinje ndi kudutsa minda mpaka kufika kwao.

Son moment préféré de la journée était juste après le coucher du soleil. Quand il faisait trop nuit pour voir les plantes, Wangari savait qu’il était l’heure de rentrer à la maison. Pour rentrer, elle devait suivre des sentiers étroits à travers champs et traverser des rivières.


Wangari anali mwana wocenjera kwambiri ndipo anali wofunitsitsa kupita kusukulu kukaphunzira. Koma makolo ake sanafune kuti kamtsikana aka kaphunzire koma kazikhala pa nyumba ndi kugwira ncthito. Pamene Wangari anali ndi zaka 7, mukulu wake wamwamuna anagonjetsa makolo awo pokambirana kuti Wangari apite kusukulu akaphunzire.

Wangari était une enfant intelligente et avait hâte d’aller à l’école. Mais sa mère et son père voulaient qu’elle reste à la maison pour les aider. Quand elle eut sept ans, son grand frère persuada ses parents de la laisser aller à l’école.


Wangaari anakonda kuphunzira kwambir chotero kuti anaphunzira kopitirira kupyolera mkuwerenga mabuku osiyanasiyana. Ndipo anakhoza kwambiri pa sukulu chotero kuti anapeza umwayi wokaphunzira ku dziko lakutali la United States of America. Wangari anasangalala kwambiri chifukwa anali kufunitsitsa kudziwa zambiri zapa dziko lapansi.

Elle aimait apprendre ! Wangari apprenait de plus en plus avec chaque livre qu’elle lisait. Elle travaillait si bien à l’école qu’elle fut invitée à étudier aux Etats Unis d’Amérique. Wangari était enthousiaste ! Elle voulait en savoir plus sur le monde.


Wangari anaphunzira zinthu zambiri pamene anali pa American Univeziti. Anaphunzira pa zomera ndi mumene zimakulira. Zimenezi zinamukumbutsa mumene anali kusewerera ndi abale ake mthunzi ya mitengo mthengo laku-dziko lokongola la Kenya.

A l’université américaine, Wangari apprit beaucoup de choses nouvelles. Elle étudia les plantes et la manière dont elles grandissent. Et elle se rappela comment elle avait grandi : en jouant avec ses frères à l’ombre des arbres dans les magnifiques forêts du Kenya.


Pamene anali kuphunzira tsiku ndi tsiku anazindikira kuti akonda anthu akwao ku Kenya. Anali kufuna kuti anthu kudziko limeneli tsiku lina akapate ufulu ndi mtendere. Ndipo anayewa dziko lakwao pamene anapitiliza ndi maphunziro. ake kwakanthawi.

Plus elle apprenait, plus elle réalisait qu’elle aimait les habitants du Kenya. Elle voulait qu’ils soient heureux et libres. Plus elle apprenait, plus elle se rappelait son foyer africain.


Anabwerera kudziko lakwao ku Kenya pamane anamaliza maphunziro ake ndipo nthawi imeneyi dziko la Kenya linali litasintha. Mapulazi akuluakulu anatenga malo ochuluka. Azimai anali kusowa kotheba nkhuni chifukwa mitengo kunalibe. Anthu anali osauka ndipo ana anali kuoneka anjala.

Quand elle eut terminé ses études, elle retourna au Kenya. Mais son pays avait changé. De larges fermes s’étendaient à travers la campagne. Les femmes n’avaient plus de bois pour cuire les aliments. Les gens étaient pauvres et les enfants avaient toujours faim.


Wangari anali kudziwa chofunika kuchita kuti athetsa mabvuto amenewa: anaphunzitsa azimai kubzyala mitengo kuchokera kumbewu. Azimai amenewa anayamba kugulitsa mitengo zao zitakula ndikupeza ndalama zosamalira ma banja awo. Chifukwa cacimenechi azimai anakhala wokondwera kwambiri ndi Wangari amene anawa thandiza kuti akhale ndi mphanvu komanso olimba.

Wangari savait ce qu’il fallait faire. Elle apprit aux femmes comment planter des arbres en utilisant des graines. Les femmes vendirent les arbres et utilisèrent l’argent pour faire vivre leurs familles. Les femmes étaient très heureuses. Wangari les avait aidées à se sentir puissantes et fortes.


Patapita zaka zambiri, mitengo zimene zinabzyalidwa zija, zinakula ndi ku panga thengo. Mitsinje inayambanso kukhala ndi madzi. Mbiri ya Wangari inafika ponseponse mu Africa. Lerolino, mitengo zamitundumitundu mamilyoni tilikuonazi zinachokera ku mbewu ya Wangari.

Avec le temps, les nouveaux arbres se transformèrent en forêts, et les rivières recommencèrent à couler. Le message de Wangari traversa toute l’Afrique. Aujourd’hui des millions d’arbres ont grandi grâce aux graines de Wangari.


Wangari anasewenzadi mwamphanvu. Chotero kuti anthu dziko lonse lapnansi anazindikila ntchito yaikula yomwe anacita, ndipo ana patsidwa mphoto yodziwika kwambiri padziko lonse lapansi. Mphoto imeneyi inali kutchedwa kuti Kulemekezedwa ndi Mtendere, ndipo anakhala mkazi woyamba mu Africa kulandila mphoto yotero.

Wangari avait travaillé dur. Partout dans le monde, les gens s’en aperçurent et lui donnèrent un prix renommé. Il s’appelle le Prix Nobel de la Paix et elle fut la première femme africaine à le recevoir.


Wangari anamwalira mu caka ca 2011, koma timamukumbukila tikamaona mtengo wokongola uliwonse mthengo.

Wangari mourut en 2011 mais nous pensons à elle à chaque fois que nous voyons un bel arbre.


Écrit par: Nicola Rijsdijk
Illustré par: Maya Marshak
Traduit par: Gridon Mwale
Lu par: Christine Mwanza
Langue: chewa
Niveau: Niveau 3
Source: A Tiny Seed: The Story of Wangari Maathai du Livre de contes africains
Licence de Creative Commons
Ce travail est autorisé sous une licence Creative Commons Attribution 4.0 non transposé.
Options
Retour à la liste des contes Téléchargement PDF