Téléchargement PDF
Retour à la liste des contes

Anansi ndi Nzelu Anansi et la sagesse

Écrit par Ghanaian folktale

Illustré par Wiehan de Jager

Traduit par Sitwe Benson Mkandawire

Lu par Christine Mwanza

Langue chewa

Niveau Niveau 3

Lire l’histoire en entier L’enregistrement audio de cette histoire est actuellement indisponible.


Matsiku amakedzana, anthu sanali kudziwa ciliconse. Sanadziwe kubzala mbeu, mwina kusoka zovala, mwina kupanga zisulo kucoka kunsimbi. Mulungu ochedwa Nyame wakumwamba anali ndi nzelu pa zonse zamziko. Nzeluzi anazisungilira bwinobwino mu poto yopangidwa ndi dothi.

Il y a longtemps, les gens ne savaient rien. Ils ne savaient pas comment ensemmencer et cultiver leurs champs, ou comment tisser, ou comment fabriquer des outils de fer. Le dieu Nyame dans le ciel avait toute la sagesse du monde. Il la gardait en sécurité dans un pot en argile.


Tsiku lina, Nyame anaganiza kupatsa Anansi poto ya nzelu. Nthawi iliyonse Anansi anayangana mupoto, anaphunziramo cinthu cimodzi catsopano. Anali okondwera kwambiri.

Un jour, Nyame décida qu’il donnerait le pot de la sagesse à Anansi. Chaque fois qu’Anansi regardait dans le pot en argile, il apprenait quelque chose de nouveau. C’était tellement excitant !


Maganizo a utani anabwera muli Anansi, “Poto yanzelu ndizaisugilira bwinobwino pamwamba pa mtengo. Mwakuti inde ndekha ndikhale ndi nzelu!” Anatenga nthambo itali nakumangilira poto pamala. Anayamba kukwela mtengo. Koma cinali covuta kukwela cifukwa poto inali kumukhumya kumyendo nthawi yonse.

Anansi, l’avide, pensa: « Je vais garder le pot en sécurité en haut d’un grand arbre. Comme ça je pourrai l’avoir à moi seul ! » Il fila un fil long, l’enroula autour du pot en argile et l’attacha à son estomac. Il commença à grimper à l’arbre. Mais c’était difficile de grimper à l’arbre avec le pot qui lui cognait les genoux tout le temps.


Pamene zonsezi zinali kucitika, mwana mwamuna mung’ono wa Anansi anali kutamba pansi pacimtengo imilire. Iye anati, “Kodi sicizakhala capafupi kukwela mtengo ngati mwamangilira poto kumusana?” Anansi anayesa kumangilira poto ya nzelu kumusana ndipo iye anakwela mtengo kosavutika.

Pendant tout ce temps, le jeune fils d’Anansi était debout en bas de l’arbre en train de regarder. « Au lieu de faire ceci, ne serait-il pas plus facile d’attacher le pot à ton dos ? » Anansi essaya d’attacher le pot rempli de sagesse à son dos et ce fut vraiment plus facile.


Posacedwa anafike pamwamba pa mtengo. Koma iye anaganiza, “Ine ndine nifunikira kukhala ndi nzelu zonse, koma apa mwana wanga ndiye anali na nzelu kucila ine!” Anansi anakalipa kwambiri paizi ndiponso, anataya poto ya nzelu pansi kucoka mucimtengo.

En peu de temps il atteignit le sommet de l’arbre. Mais il arrêta et pensa, « Je suis censé être celui qui a toute la sagesse et voici que mon fils est plus sage que moi ! » Anansi était tellement fâché à propos de ceci qu’il lança le pot en argile en bas de l’arbre.


Poto yanzelu inang’ambika mutuzidunswa pamene inafika pansi. Nzelu zinafarisidwa ku munthu aliyonse. Ndiye mwamene anthu anaphunzilira kulima, kusoka zovala, kupanga zisulo za nsimba ndi zinthu zina zamene anthu aziwa kucita.

Le pot se cassa en mille morceaux sur le sol. La sagesse fut accessible à tous. Et c’est ainsi que les gens apprirent à cultiver, tisser, fabriquer des outils de fer, et toutes les autres choses que les gens savent faire.


Écrit par: Ghanaian folktale
Illustré par: Wiehan de Jager
Traduit par: Sitwe Benson Mkandawire
Lu par: Christine Mwanza
Langue: chewa
Niveau: Niveau 3
Source: Anansi and Wisdom du Livre de contes africains
Licence de Creative Commons
Ce travail est autorisé sous une licence Creative Commons Attribution 3.0 non transposé.
Options
Retour à la liste des contes Téléchargement PDF