Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Mwana wa Bulu El Niño Burro

Texto Lindiwe Matshikiza

Ilustraciones Meghan Judge

Translated by David Sani Mwanza

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 3

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Kanali kamwana kakakazi kang’ono komwe kanaona cinthu ca maonekedwe odabwitsa patali.

Una niña pequeña fue la primera en ver una figura misteriosa a lo lejos.


Pamane cinthu cinabwela pafupi, anaona kuti anali mzimai omwe anali ndi mimba yaikulu.

Mientras la figura se acercaba, la niña se dio cuenta que era una mujer embarazada a punto de dar a luz.


Mwamanyazi koma mopanda mantha, kamwana kanasendela pafupi ndi mzimai. “Tifunika kuwasunga,” anthu a kamwana kakazi anaganizila. “Tizamusunga ndi mwana wake bwino-bwino.

Tímida pero valientemente, la pequeña niña se acercó a la mujer. “Tenemos que cuidar de ella,” decidieron los familiares de la niña pequeña. “Ella y su bebé estarán a salvo con nosotros”.


Mwana anali pafupi kubadwa. “Kankha!” “Bwelesani zovimba!” “Manzi!” “Kankhaaaa!!!”

Al poco tiempo, el bebé empezó a nacer. “¡Puja!” “¡Traigan mantas!” “¡Agua!” “¡¡¡Puuuuujjjjjaaa!!!”


Koma pamene anaona mwana wakhanda, aliyense analumpha modabwa. “Bulu?!”

Pero cuando vieron al recién nacido, todos se llevaron una gran sorpresa. “¡¿Un burro?!”


Aliyense anayamba kukangana. “Tinanena kuti tizasunga make pamozi ndi mwana wake bwino-bwino, ndipo tizacita motelo,” ena anatelo. “Koma azatibweletsela soka!” enanso ananena.

Todos empezaron a discutir. “Prometimos que cuidaríamos de la madre y su hijo, y eso es lo que haremos,” decían algunos. “¡Pero ellos nos van a traer mala suerte!” decían otros.


Cifukwa ca ico, mzimai anakhalanso yekha. Anabvutika kuganiza zomwe azacita ndi mwana wodabwisa. Anabvutika kuziganizila cocita.

Y así fue como la madre volvió a quedar sola otra vez. Se preguntaba qué hacer con este extraño bebé. Se preguntaba qué hacer consigo misma.


Koma pothela, anavomela kuti bulu anali mwana wake ndipo anali mai wake.

Pero finalmente tuvo que aceptar que ese era su bebé y que ella era su madre.


Tsopano, ngati mwana anakhala cimodzimodzi, ndi thupi ing’ono, zinthu zinakakhalako mosiyana. Koma bulu anakula ndi kukula kufikila nthawi yomwe sankakhala pa msana pa mai wake. Ndipo mkhalidwe wake unasiyana ndi munthu. Amai ake anali olema nthawi zamblili komanso aukali. Nthawi zina, anatuma mwana kucita nchito zomwe zinafunikila kucitika ndi nyama.

Si el niño se hubiera quedado del mismo tamaño, todo habría sido diferente. Pero el niño burro creció y creció hasta que su madre no pudo cargarlo más en su espalda. Y no importaba cuánto lo intentase, el niño burro no lograba comportarse como un niño humano. Su madre se la pasaba cansada y frustrada. A veces ella le ordenaba hacer trabajo de animales.


Msokonezo ndi mkwiyo unakula mu mtima wa bulu. Anali kulephela kucita zilizonse. Analephela kukhala ndi mkhalidwe weni weni. Anali okwiya kotelo kuti, tsiku lina, anamenyela amai ake pansi.

Burro sentía cada vez más confusión y rabia. Que no podía hacer esto, que no podía hacer aquello. Que él no podía ser esto ni aquello. Un día se puso tan furioso que botó a su madre al suelo de una patada.


Bulu anacita manyazi. Anayamba kuthawila kutali komwe angathe kupita ndipo anatelo mwmusanga.

Burro se sintió lleno de vergüenza. Corrió tan rápido y lejos como pudo.


Pa nthawi imene analeka kuthamanga, unali usiku, Bulu anasowa. “Hee, hyu?” ananong’oneza ku mdima. Anafika pamathelo. Anayamba kusanduka ka bola kokhwima. Anagona mu tulo twatukulu twa mabvuto.

Cuando dejó de correr, ya era de noche y Burro estaba perdido. “¿Hiaaa?” susurró en la oscuridad. “¿Hiaaa?” le respondió su eco. Estaba solo. Se acurrucó y cayó rendido en un sueño profundo e intranquilo.


Bulu anauka ndi kupeza nkhalamba ili kumuyangana. Anayangana mu maso a nkhalambayo ndi kuyamba kukhala ndi ciyembekezo.

Cuando Burro despertó, había un extraño anciano mirándolo. Burro le miró a los ojos y comenzó a sentir una chispa de esperanza.


Bulu anapita kukakhala ndi nkhalamba ija, imene inam’phunzitsa njila zambili zomwe angakhalilemo. Bulu anamvetsela ndi kuphunzila, cimodzi-modzi nkhalamba nayenso inamvetsela ndi kuphunzila. Anathandizana ndipo anaseka pamodzi.

Burro se fue a vivir con el anciano, quien le enseñó muchas formas diferentes de sobrevivir. Burro escuchaba y aprendía, y lo mismo hacía el anciano. Se ayudaban y reían juntos.


Tsiku lina m’mawa, nkhalamba inapempha Bulu kuti ainyamule kuipeleka pa mwamba pa phili.

Una mañana, el anciano le pidió a Burro que lo llevara hasta la cima de una montaña.


Pamwamba pa mithambo, anagona. Bulu analota kuti amai ake anali kudwala ndipo anali kumuitana. Ndipo pamene anauka…

Se quedaron dormidos más arriba de las nubes. Burro soñó que su madre estaba enferma y que lo llamaba. Y cuando despertó…


… Mithambo inasowa pamozi ndi mzake, nkalamba ija.

…las nubes habían desaparecido junto con su amigo, el anciano.


Bulu pomaliza anadziwa zomwe anafunika kucita.

Burro finalmente se dio cuenta de lo que tenía que hacer.


Bulu anapeza amai ake, okha ali kulilila mwana wao wosowa. Anapenyana kwakanthawi. Kenaka anakumbatilana mwamphamvu.

Burro encontró a su madre, sola y llorando por su hijo perdido. Se quedaron mirándose a los ojos por largo tiempo. Luego se abrazaron muy apretadamente.


Bulu ndi amai ake akulila pamozi ndipo anapeza njila zosiyana-siyana zokhalilamo pamodzi. Pang’ono pang’ono, onse anthu okhala pafupi nao, mabanja lao anayamba kukhala nao pamozi mopanda vuto leni-leni.

El hijo burro y su madre ya llevan tiempo creciendo juntos y han aprendido a convivir. Lentamente, otras familias se han instalado a vivir cerca de ellos.


Texto: Lindiwe Matshikiza
Ilustraciones: Meghan Judge
Translated by: David Sani Mwanza
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 3
Fuente: Donkey Child del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 4.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF