Schaltfläche PDF
Zurück zur Geschichteliste

Nyimbo ya Sakima Sakimas Lied

Geschrieben von Ursula Nafula

Illustriert von Peris Wachuka

Übersetzt von Sitwe Benson Mkandawire

Gelesen von Christine Mwanza

Sprache Nyanja

Niveau Niveau 3

Vollständige Geschichte erzählen Zu dieser Geschichte ist noch kein Audio verfügbar.


Sakima anali kukhala ndi makolo ake ndi mlongo wake wa zaka zakubadwa zinai. Anakhala pa malo a munthu wolemela, Nyumba yao inali ya uzu pothera pa mzere wa mitengo.

Sakima lebte zusammen mit seinen Eltern und seiner vier Jahre alten Schwester. Sie lebten auf dem Land eines reichen Mannes. Ihre grasbedeckte Hütte stand an einer Baumreihe.


Pamene Sakima anali ndi zaka zitatu, anadwala ndipo anakhala wa khungu. Sakima anali ndi matalanta.

Als Sakima drei Jahre alt war, wurde er krank und erblindete. Sakima war ein talentierter Junge.


Sakima anali kukwanisa kuchita zinthu zambiri zomwe ana a zaka 6 sankakwanisa kuchita.Mwachisanzo, anali kukhala ndi anthu akalu a m’mudzi ndi kukamba zinthu zofunikira.

Sakima tat viele Dinge, die andere sechsjährige Jungen nicht taten. Zum Beispiel konnte er mit den älteren Dorfbewohnern zusammensitzen und wichtige Themen besprechen.


Makolo a Sakima anali kusewenza pa nyumba ya bambo wolemera. Anachoka panyumba m’mamawa ndi kubwelela kunyumba. Sakima anali kukhala ndi mlongo wake.

Sakimas Eltern arbeiteten im Haus des reichen Manns. Sie gingen früh am Morgen zur Arbeit und kamen spät am Abend zurück. Sakima blieb bei seiner Schwester.


Sakima anakonda kuimba nyimbo. Tsiku lina, amai ake anamufunsa, “kodi uphunzila kuti nyimbo izi, Sakima?”

Sakima liebte es, Lieder zu singen. Eines Tages fragte seine Mutter ihn: „Wo lernst du diese Lieder, Sakima?“


Sakima anayankha, “zimabwela chabe, amai. Ndimazimvela m’mutu mwanga ndipo ndimaziimba.”

Sakima antwortete: „Sie kommen mir einfach, Mutter. Ich höre sie in meinem Kopf und dann singe ich los.“


Sakima anakonda kuimbila mlongo wake wam’gono, makamaka ngati anali wokwiya. Mlongo wake anamvelera ku nyimbo yake yapa mtima. Anatothozedwa.

Sakima sang gern für seine kleine Schwester, besonders, wenn sie Hunger hatte. Seine Schwester hörte ihm beim Singen seines Lieblingsliedes zu. Sie wiegte im Takt zu der beruhigenden Melodie.


“Imbanso, Sakima,” mlongo wake anamupempha. Sakima ankavomela ndi kuimbanso mobwelezera.

„Kannst du es wieder und wieder singen, Sakima?“, bat ihn seine Schwester. Sakima stimmte zu und sang immer wieder.


Tsiku lina pamene makolo ake anbwelera ku nyumba, anakhala chete. Sakima anadziwa kuti kunali vuto.

Eines Abends als seine Eltern nach Hause kamen, waren sie sehr still. Sakima wusste, dass etwas nicht in Ordnung war.


“Kodi nichani chalakwika, amai, atate?” sakima anafunsa. Sakima anamvela kuti mwana wa bambo wolemera anasowa ndi bambo wake anali ndi chisoni.

„Was ist los, Mutter, Vater?“, fragte Sakima. Sakima erfuhr, dass der Sohn des reichen Mannes vermisst wurde. Der Mann war sehr traurig und einsam.


“Ndingawaimbile. Angakondwelenso,” Sakima anaudza makolo ake. Koma makolo ake sanamuvokeze naye. “Ndi munthu wolemela kwambiri. Iwe uli wa khungu chabe. Uganiza kuti nyimbo yako izamuthandiza?”

„Ich kann für ihn singen. Vielleicht stimmt ihn das wieder glücklich“, erzählte Sakima seinen Eltern. Aber seine Eltern lehnten ab: „Er ist sehr reich. Du bist nur ein blinder Junge. Glaubst du ein Lied hilft ihm?“


Angakhale choncho, Sakima sanaleke. Mlongo wake wamng’ono anamupasa mphamvu. Iye anati, “Nyimbo za Sakima zimandilimbikitsa pamene ndili okwiya. Zizalimbikitsanso bambo wolemela.

Trotzdem gab Sakima nicht auf. Seine kleine Schwester unterstützte ihn. Sie meinte: „Sakimas Lieder trösten mich, wenn ich Hunger habe. Sie werden auch den reichen Mann trösten.“


Tsiku lotsatilapo, Sakima anapempha mlongo wake kumupeleka ku nyumba ya bambo wolemela.

Am nächsten Tag bat Sakima seine kleine Schwester ihn zum Haus des reichen Mannes zu bringen.


Anaimilila pa pafupi ndi dzenera ndi kuyamba kimba nyimbo yake yapa mtima. Posachedwa, mutu wa bambo wolemela unayamba kuonekela pa dezenera lalikulu.

Er stand unter einem der großen Fenster und begann sein Lieblingslied zu singen. Langsam wurde das Gesicht des reichen Mannes am großen Fenster sichtbar.


Anchito analeka zomwe anali kuchita. Anamvesela ku nyimbo ya Sakima yabwino. Koma bambo wina anati, “Kulibe omwe anakwanisapo kutonthoza akulu anchito. Kodi mnyamata wakhungu uyu aganiza kuti azawatonthoza?”.

Die Arbeiter unterbrachen ihre Arbeit. Sie hörten Sakimas wunderschönem Lied zu. Aber ein Mann meinte: „Niemand hat es geschafft, den Chef zu trösten. Glaubt dieser blinde Junge, dass er ihn trösten kann?“


Sakima anasiliza kuimba nyimbo yake ndipo anatembenuka kufuna kubwelela kunyumba. Koma bambo wolemela atuluka naumuuza nati, “Chonde, imbanso nyimbo.”

Sakima sang das Lied zu Ende und wollte sich auf den Heimweg machen. Aber der reiche Mann eilte aus dem Haus und sagte: „Bitte, sing noch einmal.“


Pa nthawi yomweyo, amuna awiri anabwela apo anyamula munthu. Anali anapeza mwana wa bambo wolemelayo atamenyedwa ndi kusiyidwa pambali pa mseu.

In dem Moment kamen zwei Männer und brachten jemanden auf einer Liege. Sie hatten den Sohn des reichen Mannes verprügelt am Straßenrand gefunden.


Bambo wolemela anakondwela kwambiri kuona mwana wake. Anapasa mphaso kwa Sakima powatonthoza. Anapeleka mwana wao ndi Sakima ku chipatala kuti Sakima akayambe kuonanso.

Der reiche Mann war so glücklich, seinen Sohn wiederzusehen. Er belohnte Sakima für seinen Trost. Er brachte seinen Sohn und Sakima ins Krankenhaus, damit Sakima seine Sehkraft wieder bekam.


Geschrieben von: Ursula Nafula
Illustriert von: Peris Wachuka
Übersetzt von: Sitwe Benson Mkandawire
Gelesen von: Christine Mwanza
Sprache: Nyanja
Niveau: Niveau 3
Quelle: Sakima's song aus African Storybook
Creative Commons Lizenz
Dieses Werk ist unter einer Creative Commons Namensnennung 4.0 Lizenz lizenziert.
Optionen
Zurück zur Geschichteliste Schaltfläche PDF