Schaltfläche PDF
Zurück zur Geschichteliste

Kambewu: Nkhani ya Wangari Maathai Ein winziges Saatkorn: Die Geschichte von Wangari Maathai

Geschrieben von Nicola Rijsdijk

Illustriert von Maya Marshak

Übersetzt von Gridon Mwale

Gelesen von Christine Mwanza

Sprache Nyanja

Niveau Niveau 3

Vollständige Geschichte erzählen Zu dieser Geschichte ist noch kein Audio verfügbar.


Pamudzi wina womangidwa pamatero ya phiri la Kenya kumwawa kwa Africa, Kunali kamtsikana kena dzina lake Wangari. Wangari ndi amai ake anali kugwira ntchito zaminda.

In einem Dorf in den Hängen des Mount Kenia in Ostafrika arbeitete ein kleines Mädchen mit ihrer Mutter auf den Feldern. Ihr Name war Wangari.


Wangari anali mtsikana wokonda kucezera pabwalo. Tisku lina Wangari anagaula mudimba mwao nabzyala tumbewu pansi pomwe panali potentha kwambiri.

Wangari liebte es, draußen zu sein. Im Gemüsegarten ihrer Familie lockerte sie den Boden mit ihrer Machete. Sie drückte kleine Saatkörner in die warme Erde.


Thawi imene anali kukonda kwambiri mtsikanayu tsiku lililonse inali pamene dzuwa litangolowa kumene. Ndipo mudima ukagwira chakuti zomera zamthengo zaleka kuoneka, Wangari anali kudziwa kuti thawi yopita ku nyumba yafika tsopano. Ndipo popita kunyumba anali kudzera njira zang’ombe, kuwoloka mitsinje ndi kudutsa minda mpaka kufika kwao.

Ihre liebste Tageszeit war nach Sonnenuntergang. Als es zu dunkel war, um die Pflanzen zu sehen, wusste Wangari, dass es Zeit war, nach Hause zu gehen. Sie folgte dem schmalen Pfad durch die Felder und überquerte dabei den Fluss.


Wangari anali mwana wocenjera kwambiri ndipo anali wofunitsitsa kupita kusukulu kukaphunzira. Koma makolo ake sanafune kuti kamtsikana aka kaphunzire koma kazikhala pa nyumba ndi kugwira ncthito. Pamene Wangari anali ndi zaka 7, mukulu wake wamwamuna anagonjetsa makolo awo pokambirana kuti Wangari apite kusukulu akaphunzire.

Wangari war ein kluges Kind und sie konnte es nicht erwarten, in die Schule zu gehen. Aber ihre Mutter und ihr Vater wollten, dass sie zu Hause blieb und ihnen im Haus half. Als sie sieben Jahre alt war, überredete ihr großer Bruder ihre Eltern, sie zur Schule gehen zu lassen.


Wangaari anakonda kuphunzira kwambir chotero kuti anaphunzira kopitirira kupyolera mkuwerenga mabuku osiyanasiyana. Ndipo anakhoza kwambiri pa sukulu chotero kuti anapeza umwayi wokaphunzira ku dziko lakutali la United States of America. Wangari anasangalala kwambiri chifukwa anali kufunitsitsa kudziwa zambiri zapa dziko lapansi.

Sie lernte gern! Wangari lernte immer mehr mit jedem Buch, das sie las. Sie war so gut in der Schule, dass sie eingeladen wurde, in den Vereinigten Staaten von Amerika zu studieren. Wangari war begeistert! Sie wollte mehr über die Welt wissen.


Wangari anaphunzira zinthu zambiri pamene anali pa American Univeziti. Anaphunzira pa zomera ndi mumene zimakulira. Zimenezi zinamukumbutsa mumene anali kusewerera ndi abale ake mthunzi ya mitengo mthengo laku-dziko lokongola la Kenya.

An der amerikanischen Universität lernte Wangari viele neue Dinge. Sie studierte Pflanzen und wie diese wuchsen. Und sie erinnerte sich, wie sie selbst wuchs: Spiele spielend mit ihren Brüdern im Schatten der Bäume in schönen kenianischen Wäldern.


Pamene anali kuphunzira tsiku ndi tsiku anazindikira kuti akonda anthu akwao ku Kenya. Anali kufuna kuti anthu kudziko limeneli tsiku lina akapate ufulu ndi mtendere. Ndipo anayewa dziko lakwao pamene anapitiliza ndi maphunziro. ake kwakanthawi.

Je mehr sie lernte, desto mehr wurde ihr klar, dass sie die Menschen in Kenia liebte. Sie wollte, dass sie frei und glücklich sind. Je mehr sie lernte, desto mehr erinnerte sie sich an ihre afrikanische Heimat.


Anabwerera kudziko lakwao ku Kenya pamane anamaliza maphunziro ake ndipo nthawi imeneyi dziko la Kenya linali litasintha. Mapulazi akuluakulu anatenga malo ochuluka. Azimai anali kusowa kotheba nkhuni chifukwa mitengo kunalibe. Anthu anali osauka ndipo ana anali kuoneka anjala.

Als sie ihr Studium beendet hatte, kehrte sie nach Kenia zurück. Aber ihr Land hatte sich verändert. Riesige Farmen erstreckten sich über das Land. Frauen hatten kein Feuerholz mehr zum Kochen. Die Menschen waren arm und die Kinder hungrig.


Wangari anali kudziwa chofunika kuchita kuti athetsa mabvuto amenewa: anaphunzitsa azimai kubzyala mitengo kuchokera kumbewu. Azimai amenewa anayamba kugulitsa mitengo zao zitakula ndikupeza ndalama zosamalira ma banja awo. Chifukwa cacimenechi azimai anakhala wokondwera kwambiri ndi Wangari amene anawa thandiza kuti akhale ndi mphanvu komanso olimba.

Wangari wusste, was zu tun war. Sie brachte den Frauen bei, wie man Bäume mit Saatkörnern pflanzt. Die Frauen verkauften die Bäumen und nahmen das Geld davon, um ihre Familien zu versorgen. Die Frauen waren sehr glücklich. Wangari hatte ihnen dabei geholfen, sich kräftig und stark zu fühlen.


Patapita zaka zambiri, mitengo zimene zinabzyalidwa zija, zinakula ndi ku panga thengo. Mitsinje inayambanso kukhala ndi madzi. Mbiri ya Wangari inafika ponseponse mu Africa. Lerolino, mitengo zamitundumitundu mamilyoni tilikuonazi zinachokera ku mbewu ya Wangari.

Mit der Zeit wuchsen die neuen Bäume zu Wäldern und die Flüsse begannen wieder zu fließen. Wangaris Botschaft verbreitet sich in ganz Afrika. Heutzutage sind Millionen Bäume aus Wangaris Saatkörnern gewachsen.


Wangari anasewenzadi mwamphanvu. Chotero kuti anthu dziko lonse lapnansi anazindikila ntchito yaikula yomwe anacita, ndipo ana patsidwa mphoto yodziwika kwambiri padziko lonse lapansi. Mphoto imeneyi inali kutchedwa kuti Kulemekezedwa ndi Mtendere, ndipo anakhala mkazi woyamba mu Africa kulandila mphoto yotero.

Wangari arbeitete schwer. Leute auf der ganzen Welt hörten von ihr und gaben ihr einen Preis. Er heißt Friedensnobelpreis und sie war die erste afrikanische Frau, die ihn jemals erhalten hat.


Wangari anamwalira mu caka ca 2011, koma timamukumbukila tikamaona mtengo wokongola uliwonse mthengo.

Wangari starb 2011, aber jedesmal, wenn wir einen schönen Baum sehen, können wir an sie denken.


Geschrieben von: Nicola Rijsdijk
Illustriert von: Maya Marshak
Übersetzt von: Gridon Mwale
Gelesen von: Christine Mwanza
Sprache: Nyanja
Niveau: Niveau 3
Quelle: A Tiny Seed: The Story of Wangari Maathai aus African Storybook
Creative Commons Lizenz
Dieses Werk ist unter einer Creative Commons Namensnennung 4.0 Lizenz lizenziert.
Optionen
Zurück zur Geschichteliste Schaltfläche PDF