Schaltfläche PDF
Zurück zur Geschichteliste

Anansi ndi Nzelu Anansi und die Weisheit

Geschrieben von Ghanaian folktale

Illustriert von Wiehan de Jager

Übersetzt von Sitwe Benson Mkandawire

Gelesen von Christine Mwanza

Sprache Nyanja

Niveau Niveau 3

Vollständige Geschichte erzählen Zu dieser Geschichte ist noch kein Audio verfügbar.


Matsiku amakedzana, anthu sanali kudziwa ciliconse. Sanadziwe kubzala mbeu, mwina kusoka zovala, mwina kupanga zisulo kucoka kunsimbi. Mulungu ochedwa Nyame wakumwamba anali ndi nzelu pa zonse zamziko. Nzeluzi anazisungilira bwinobwino mu poto yopangidwa ndi dothi.

Vor langer, langer Zeit wussten die Menschen gar nichts. Sie wussten nicht, wie man Pflanzen anbaut, wie man Tücher webt, oder wie man Eisenwerkzeuge herstellt. Der Gott Nyame oben im Himmel hatte die ganze Weisheit der Welt. Er bewahrte sie sicher in einem Tontopf auf.


Tsiku lina, Nyame anaganiza kupatsa Anansi poto ya nzelu. Nthawi iliyonse Anansi anayangana mupoto, anaphunziramo cinthu cimodzi catsopano. Anali okondwera kwambiri.

Eines Tages beschloss Nyame, den Tontopf Anansi zu geben. Jedes Mal, wenn Anansi in den Topf schaute, lernte er etwas Neues. Es war so aufregend!


Maganizo a utani anabwera muli Anansi, “Poto yanzelu ndizaisugilira bwinobwino pamwamba pa mtengo. Mwakuti inde ndekha ndikhale ndi nzelu!” Anatenga nthambo itali nakumangilira poto pamala. Anayamba kukwela mtengo. Koma cinali covuta kukwela cifukwa poto inali kumukhumya kumyendo nthawi yonse.

Gierig dachte Anansi: „Ich werde den Topf sicher im Gipfel eines Baumes aufbewahren. So habe ich ihn ganz für mich allein!“ Er spann einen langen Zwirn, wickelte ihn um den Tontopf und band ihn um seinen Bauch. Er begann, den Baum hinaufzuklettern. Aber es war schwer den Baum so hinaufzuklettern, da der Topf ständig gegen seine Knie stieß.


Pamene zonsezi zinali kucitika, mwana mwamuna mung’ono wa Anansi anali kutamba pansi pacimtengo imilire. Iye anati, “Kodi sicizakhala capafupi kukwela mtengo ngati mwamangilira poto kumusana?” Anansi anayesa kumangilira poto ya nzelu kumusana ndipo iye anakwela mtengo kosavutika.

Die ganze Zeit hatte Anansis junger Sohn unten am Baum gestanden und ihm zugeschaut: „Wäre es nicht leichter, wenn du dir den Topf stattdessen auf den Rücken bindest?“ Anansi versuchte es mit dem Topf auf dem Rücken und es ging in der Tat viel besser.


Posacedwa anafike pamwamba pa mtengo. Koma iye anaganiza, “Ine ndine nifunikira kukhala ndi nzelu zonse, koma apa mwana wanga ndiye anali na nzelu kucila ine!” Anansi anakalipa kwambiri paizi ndiponso, anataya poto ya nzelu pansi kucoka mucimtengo.

Im Nu erklomm Anansi die Baumspitze. Aber dann hielt er inne und dachte: „Ich soll derjenige mit der ganzen Weisheit sein und eben war mein Sohn schlauer als ich!“ Dies verärgerte Anansi so sehr, dass er den Tontopf vom Baum hinunter warf.


Poto yanzelu inang’ambika mutuzidunswa pamene inafika pansi. Nzelu zinafarisidwa ku munthu aliyonse. Ndiye mwamene anthu anaphunzilira kulima, kusoka zovala, kupanga zisulo za nsimba ndi zinthu zina zamene anthu aziwa kucita.

Am Boden zerbrach er in viele Stücke. Die Weisheit gehörte nun allen. Und so lernten die Menschen, Landwirtschaft zu betreiben, Tücher zu weben, Eisenwerkzeuge herzustellen und alles andere, was wir heute wissen.


Geschrieben von: Ghanaian folktale
Illustriert von: Wiehan de Jager
Übersetzt von: Sitwe Benson Mkandawire
Gelesen von: Christine Mwanza
Sprache: Nyanja
Niveau: Niveau 3
Quelle: Anansi and Wisdom aus African Storybook
Creative Commons Lizenz
Dieses Werk ist unter einer Creative Commons Namensnennung 3.0 Lizenz lizenziert.
Optionen
Zurück zur Geschichteliste Schaltfläche PDF