Mudzi wanga unali ndi mabvuto ambili. Timaima m’mzele wautali umodzi kutunga madzi pa pompi imodzi.
我的村庄面临很多问题。村里只有一个水龙头,我们每天都要排很长的队伍去接水。
Tinayembekezela zakudya zopelekedwa ndi ena.
我们等着别人接济食物给我们吃。
Tinakhoma manyumba athu mwamsanga cifukwa coopa akawalala.
每天晚上,我们因为害怕有小偷,所以都早早地锁上了门。
Ana ambili analeka sukulu.
中途辍学的孩子也不少。
Atsikana ang’ono ang’ono anasewenza maganyu m’midzi ina.
年轻的女孩被迫到别的村庄去做女佣。
Anyamata ang’ono ang’ono anali kuyendayenda m’midzi ina ndipo ena anali kuchita ganyu m’minda ya ena.
年轻的男孩不是成天在村子里游荡,就是到别人的农场里打工。
Pamene mphepo ikuntha, mapepala opanda nchito anapacikika pa mitengo ndi mipanda.
起风的时候,废纸到处乱飞,挂在树梢和篱笆上。
Anthu anacekedwa ndi magalasi oonongeka amane anataidwa mosasamala.
碎玻璃扔得到处都是,很多人都被碎玻璃划伤了。
Ndipo tsiku lina, pompi inauma ndipo migomo yathu inalibe madzi.
终于有一天,水龙头干涸了,人们接不到水了。
Atate anga anayenda khomo ndi khomo kupempha anthu kuti apite ku msonkhano wa m’mudzi.
我的爸爸一家一家地劝说,召集村里的居民们开会。
Anthu anasonkhana pansi pa mtengo ukulu ndipo anamvesela.
人们聚到一棵大树下,准备开会。
Atate anga anaima nati, “Tifunika kusewenzela pamozi kuti tithetse mabvuto athu.”
我爸爸站起来,说:“我们必须团结起来,一起解决我们的问题。”
Juma wa zaka zisanu ndi zitatu, omwe anakhala pa nthambi ya mtengo anakuwa nati “Ndingathandize ndi kusesa.”
八岁的珠玛坐在树干上,大声说:“我可以帮忙清理村庄。”
Mai m’mozi anati “azimai angasewenze pamozi ndi ine kuti tilime zakudya.”
一个女人站起来说:“我可以找一些妇女,一起种庄稼。”
Bambo wina anaimilila nati “Amuna azakumba citsime.”
又有一个男人站起来说:“男人们可以帮着打井。”
Tonse tinakuwa ndi mau amozi ndikuti, “tifunika kusintha myoyo yathu.” Kucoka pa tsiku lija, tinasewenzela pamozi kuthetsa mabvuto athu.
我们异口同声地说:“我们必须改变我们的生活。”从那天开始,大伙儿都齐心协力,解决问题。