Mbuzi, Galu ndi Ng’ombe anali mabwenzi kwambili. Tsiku lina, anapita paulendo ndi galimoto.
山羊、野狗、和水牛是很要好的朋友。有一天,他们一起坐出租车。
Pamene anafika pothela pa ulendo wao, mtekenya anawafunsa kuti alipile ndalama. Ng’ombe inalipila yake.
当他们到了目的地的时候,司机叫他们交车费。水牛把她自己的那份交了。
Galu analipila ndalama yopitililapo chifukwa analibe ndalama yoyenela.
野狗没有带零钱,所以他就多给了一点儿。
Mtekenya anali pafupi kupatsa Galu chenji yake pamene mbuzi inathawa kopanda kulipila.
司机正要找钱给野狗,没想到山羊没有给钱就跑掉了。
Mtekenya anakalipa kwambili. Anayenda popanda kupatsa Galu chenji yake.
司机很生气,结果他没有给野狗找钱就开走了。
Ndiye cifukwa cake, ngakhale lelo lomwe, Galu amathamangila galimoto kuona mkati ndi kupeza mtekenya amene ali ndi chenji yake.
所以,现在你可以看到野狗看到车子就拼命追上去,因为他想叫司机给他找钱。
Mbuzi imathawa ikamvela galimoto. Imaopa kuti angaimangidwe chifukwa siinalipile mtekenya.
山羊呢,一听到有车来就吓得赶快逃走,因为她怕没交车费被人抓起来。
Ndipo Ng’ombe siimaikako nzelu ngati galimoto ili kubwela. Ng’ombe imayenda pang’ono pang’ono cifukwa idziwa kuti inalipila ndalama mokwana.
可是水牛听到车来一点儿都不急。她不慌不忙地过马路,因为她知道她已经把她自己那份交了。