Mbuzi, Galu ndi Ng’ombe anali mabwenzi kwambili. Tsiku lina, anapita paulendo ndi galimoto.
La Cabra, el Perro y la Vaca eran muy buenos amigos. Un día se fueron de viaje en un taxi.
Pamene anafika pothela pa ulendo wao, mtekenya anawafunsa kuti alipile ndalama. Ng’ombe inalipila yake.
Al finalizar el viaje, el chofer les pidió que pagaran sus pasajes. La Vaca pagó su pasaje.
Galu analipila ndalama yopitililapo chifukwa analibe ndalama yoyenela.
El Perro pagó un poco más, porque no tenía la cantidad de dinero exacta.
Mtekenya anali pafupi kupatsa Galu chenji yake pamene mbuzi inathawa kopanda kulipila.
El chofer estaba a punto de darle el vuelto al Perro, cuando la Cabra se arrancó sin pagar nada.
Mtekenya anakalipa kwambili. Anayenda popanda kupatsa Galu chenji yake.
El chofer estaba muy enojado. Se fue sin darle el cambio al Perro.
Ndiye cifukwa cake, ngakhale lelo lomwe, Galu amathamangila galimoto kuona mkati ndi kupeza mtekenya amene ali ndi chenji yake.
Debido a esto, hasta el día de hoy, el Perro corre detrás del carro para mirar adentro y encontrar al chofer que le debe su vuelto.
Mbuzi imathawa ikamvela galimoto. Imaopa kuti angaimangidwe chifukwa siinalipile mtekenya.
La cabra huye cuando escucha el sonido de un carro. Ella tiene miedo de ser arrestada por no haber pagado su pasaje.
Ndipo Ng’ombe siimaikako nzelu ngati galimoto ili kubwela. Ng’ombe imayenda pang’ono pang’ono cifukwa idziwa kuti inalipila ndalama mokwana.
Y la vaca no se molesta cuando un carro se acerca, incluso se toma su tiempo para cruzar la calle, porque ella sabe que pagó su pasaje completo.