تحميل بصيغة PDF
العودة لقائمة القصص

Kambewu: Nkhani ya Wangari Maathai البذرة الصغيرة – حكاية ونقاري ماتهاي

كُتِب بواسطة Nicola Rijsdijk

رسمة بواسطة Maya Marshak

بترجمة Gridon Mwale

لغة الشيشيوا

مستوى المستوى 3

سرد للقصة كاملة الصوت لهذه القصة غير متوفر.


Pamudzi wina womangidwa pamatero ya phiri la Kenya kumwawa kwa Africa, Kunali kamtsikana kena dzina lake Wangari. Wangari ndi amai ake anali kugwira ntchito zaminda.

في قرية على منحدر جبل كينيا بشرق إفريقيا، كان هناك فتاة صغيرة تدعى ونقاري تعمل مع أمها في الحقول.


Wangari anali mtsikana wokonda kucezera pabwalo. Tisku lina Wangari anagaula mudimba mwao nabzyala tumbewu pansi pomwe panali potentha kwambiri.

كانت ونقاري تحب الحياة خارج البيت فكنت أراها تعمل في حديقة منزل العائلة، تشق التربة بعصاها وتغرس الحبات الصغيرة في أديم الأرض الدافئ.


Thawi imene anali kukonda kwambiri mtsikanayu tsiku lililonse inali pamene dzuwa litangolowa kumene. Ndipo mudima ukagwira chakuti zomera zamthengo zaleka kuoneka, Wangari anali kudziwa kuti thawi yopita ku nyumba yafika tsopano. Ndipo popita kunyumba anali kudzera njira zang’ombe, kuwoloka mitsinje ndi kudutsa minda mpaka kufika kwao.

وكانت أفضل فترات اليوم لديها هي فترة ما بعد الغروب، حين يسدل الليل ستاره ويحل الظلام. عندها تعرف ونقاري أن الوقت قد حان للعودة إلى المنزل فتحث خطاها إلى البيت متبعة المسالك الضيقة عبر الحقول، عابرة الأنهار التي تعترض طريقها.


Wangari anali mwana wocenjera kwambiri ndipo anali wofunitsitsa kupita kusukulu kukaphunzira. Koma makolo ake sanafune kuti kamtsikana aka kaphunzire koma kazikhala pa nyumba ndi kugwira ncthito. Pamene Wangari anali ndi zaka 7, mukulu wake wamwamuna anagonjetsa makolo awo pokambirana kuti Wangari apite kusukulu akaphunzire.

كانت ونقاري فتاة ذكية وكانت شغوفة بالذهاب إلى المدرسة لكن أمها وأباها أراداها أن تبقى في المنزل لإعانتهما. لكن عندما بلغت سن السابعة من عمرها استطاع أخوها الأكبر إقناع والديها بأن يسمحا لها بالالتحاق بالمدرسة.


Wangaari anakonda kuphunzira kwambir chotero kuti anaphunzira kopitirira kupyolera mkuwerenga mabuku osiyanasiyana. Ndipo anakhoza kwambiri pa sukulu chotero kuti anapeza umwayi wokaphunzira ku dziko lakutali la United States of America. Wangari anasangalala kwambiri chifukwa anali kufunitsitsa kudziwa zambiri zapa dziko lapansi.

شغفت ونقاري بالدراسة وكانت كلما قرأت كتاباً زاد شغفها بالتعلم. وحققت ونقاري نتائج باهرة في المدرسة مما مكنها من مواصلة دراستها بالولايات المتحدة الأمريكية. فرحت الفتاة كثيرا وزادت رغبتها في التعرف على العالم.


Wangari anaphunzira zinthu zambiri pamene anali pa American Univeziti. Anaphunzira pa zomera ndi mumene zimakulira. Zimenezi zinamukumbutsa mumene anali kusewerera ndi abale ake mthunzi ya mitengo mthengo laku-dziko lokongola la Kenya.

تعلمت ونقاري العديد من الأشياء الجديدة في الجامعة الأمريكية وتلقت دروسا حول النباتات وكيفية نموها. استرجعت ونقاري ذكريات طفولتها عندما كانت تلعب مع إخوتها تحت ظل الأشجار في غابات كينيا الجميلة.


Pamene anali kuphunzira tsiku ndi tsiku anazindikira kuti akonda anthu akwao ku Kenya. Anali kufuna kuti anthu kudziko limeneli tsiku lina akapate ufulu ndi mtendere. Ndipo anayewa dziko lakwao pamene anapitiliza ndi maphunziro. ake kwakanthawi.

وبقدر ما كانت تزداد علماً ودراسة بقدر ما كان حبها لشعب كينيا يزداد ويتعمق. كانت تريدهم أن يكونوا سعداء وأحراراً، فكانت كلما زاد علمها، زاد تعلقها بموطنها.


Anabwerera kudziko lakwao ku Kenya pamane anamaliza maphunziro ake ndipo nthawi imeneyi dziko la Kenya linali litasintha. Mapulazi akuluakulu anatenga malo ochuluka. Azimai anali kusowa kotheba nkhuni chifukwa mitengo kunalibe. Anthu anali osauka ndipo ana anali kuoneka anjala.

وعندما أنهت ونقاري دراستها رجعت إلى كينيا، لكنها اكتشفت أن كينيا قد تغيرت: كانت المزارع الشاسعة تمتد في جميع أنحاء الأرض بينما لم يكن للنساء حطباً لطهي الطعام وكان الناس فقراء والصغار جياعاً.


Wangari anali kudziwa chofunika kuchita kuti athetsa mabvuto amenewa: anaphunzitsa azimai kubzyala mitengo kuchokera kumbewu. Azimai amenewa anayamba kugulitsa mitengo zao zitakula ndikupeza ndalama zosamalira ma banja awo. Chifukwa cacimenechi azimai anakhala wokondwera kwambiri ndi Wangari amene anawa thandiza kuti akhale ndi mphanvu komanso olimba.

عرفت ونقاري ما يجب عليها فعله. فعلمت النساء كيف يزرعن البذور، ونمت الأشجار وأصبحت النساء يبعن هذه الأشجار وبثمنها يعتنين بعائلاتهن. شعرت النساء بالسعادة، فقد ساعدتهن ونقاري على أن يكنَّ قويات فاعلات.


Patapita zaka zambiri, mitengo zimene zinabzyalidwa zija, zinakula ndi ku panga thengo. Mitsinje inayambanso kukhala ndi madzi. Mbiri ya Wangari inafika ponseponse mu Africa. Lerolino, mitengo zamitundumitundu mamilyoni tilikuonazi zinachokera ku mbewu ya Wangari.

وبمرور الزمن، تحولت الأشجار إلى غابات وجرت الأنهار بالماء من جديد وانتشرت رسالة ونقاري في كامل أرجاء إفريقيا، ونمت ملايين الأشجار بفضل بذور ونقاري.


Wangari anasewenzadi mwamphanvu. Chotero kuti anthu dziko lonse lapnansi anazindikila ntchito yaikula yomwe anacita, ndipo ana patsidwa mphoto yodziwika kwambiri padziko lonse lapansi. Mphoto imeneyi inali kutchedwa kuti Kulemekezedwa ndi Mtendere, ndipo anakhala mkazi woyamba mu Africa kulandila mphoto yotero.

لاحظ الناس في جميع أنحاء العالم تفاني ونقاري في العمل وقدموا لها جائزة شهيرة: إنها جائزة نوبل للسلام والتي كانت ونقاري أول امرأة افريقية تحصل عليها.


Wangari anamwalira mu caka ca 2011, koma timamukumbukila tikamaona mtengo wokongola uliwonse mthengo.

توفيت ونقاري سنة 2011، لكننا نتذكرها في كل شجرة جميلة نراها حولنا.


كُتِب بواسطة: Nicola Rijsdijk
رسمة بواسطة: Maya Marshak
بترجمة: Gridon Mwale
لغة: الشيشيوا
مستوى: المستوى 3
المصدر: A Tiny Seed: The Story of Wangari Maathai از القصص الأفريقية القصيرة
رخصة المشاع الإبداعي
تحت مجوز المشاع الإبداعي نَسب المُصنَّف 4.0 دولي کریتز کامنز به نشر رسید.
خيارات
العودة لقائمة القصص تحميل بصيغة PDF