تحميل بصيغة PDF
العودة لقائمة القصص

Anansi ndi Nzelu أنانسي و الحكمة

كُتِب بواسطة Ghanaian folktale

رسمة بواسطة Wiehan de Jager

بترجمة Sitwe Benson Mkandawire

لغة الشيشيوا

مستوى المستوى 3

سرد للقصة كاملة الصوت لهذه القصة غير متوفر.


Matsiku amakedzana, anthu sanali kudziwa ciliconse. Sanadziwe kubzala mbeu, mwina kusoka zovala, mwina kupanga zisulo kucoka kunsimbi. Mulungu ochedwa Nyame wakumwamba anali ndi nzelu pa zonse zamziko. Nzeluzi anazisungilira bwinobwino mu poto yopangidwa ndi dothi.

في قديم الزمان، كان الناس لا يعرفون شيئا. كانوا لا يعرفون طريقة زراعة المحاصيل، أو نسج الأقمشة، أو صناعة الأدوات الحديدية. كان هناك الإله نيام في السماء وكان يملك كل الحكمة الموجودة في العالم. وكان محتفظا بها في وعاء من الفخار.


Tsiku lina, Nyame anaganiza kupatsa Anansi poto ya nzelu. Nthawi iliyonse Anansi anayangana mupoto, anaphunziramo cinthu cimodzi catsopano. Anali okondwera kwambiri.

في يوم من الأيام، قرر نيام أن يعطي وعاء الحكمة إلى أنانسي. في كل مرة كان أنانسي ينظر في وعاء الفخار، كان يتعلم شيئا جديدا. كان أمرا مثيرا!


Maganizo a utani anabwera muli Anansi, “Poto yanzelu ndizaisugilira bwinobwino pamwamba pa mtengo. Mwakuti inde ndekha ndikhale ndi nzelu!”. Anatenga nthambo itali nakumangilira poto pamala. Anayamba kukwela mtengo. Koma cinali covuta kukwela cifukwa poto inali kumukhumya kumyendo nthawi yonse.

فكر الجشع أنانسي: “أنا سوف أحتفظ بالوعاء في مكان آمن في أعلى شجرة طويلة. بعد ذلك يمكن أن يكون كل شيء لنفسي!” ونسج خيط طويل، ولفه حول وعاء الطين، وربطه إلى بطنه. بدأ تسلق الشجرة. ولكن كان من الصعب تسلق الشجرة والوعاء يخبط في ركبتيه طوال الوقت.


Pamene zonsezi zinali kucitika, mwana mwamuna mung’ono wa Anansi anali kutamba pansi pacimtengo imilire. Iye anati, “Kodi sicizakhala capafupi kukwela mtengo ngati mwamangilira poto kumusana?” Anansi anayesa kumangilira poto ya nzelu kumusana ndipo iye anakwela mtengo kosavutika.

خلال كل هذا الوقت كان ابن أنانسي الصغير يشاهد من أسفل الشجرة. وقال: “ألن يكون من الأسهل تسلق الشجرة إذا كان الوعاء مربوطا إلى ظهرك بدلا من بطنك؟” حاول أنانسي ربط وعاء الفخار المليء بالحكمة إلى ظهره، وأصبح فعلا تسلق الشجرة أسهل.


Posacedwa anafike pamwamba pa mtengo. Koma iye anaganiza, “Ine ndine nifunikira kukhala ndi nzelu zonse, koma apa mwana wanga ndiye anali na nzelu kucila ine!” Anansi anakalipa kwambiri paizi ndiponso, anataya poto ya nzelu pansi kucoka mucimtengo.

خلال وقت قصير وصل إلى أعلى الشجرة. ولكن بعد ذلك توقف وفكر، “أنا من المفترض أن أكون صاحب كل الحكمة، وهنا كان ابني أذكى مني!” كان أنانسي غاضب جدا وألقى وعاء الفخار إلى أسفل الشجرة.


Poto yanzelu inang’ambika mutuzidunswa pamene inafika pansi. Nzelu zinafarisidwa ku munthu aliyonse. Ndiye mwamene anthu anaphunzilira kulima, kusoka zovala, kupanga zisulo za nsimba ndi zinthu zina zamene anthu aziwa kucita.

تحطم الوعاء إلى قطع صغيرة على الأرض. وأصبحت الحكمة للجميع لكي يتشاركوها. وهكذا تعلم الناس الفلاحة، ونسج الأقمشة، وصناعة الأدوات الحديدية، وجميع الأشياء الأخرى التي يعرف الناس كيفية القيام بها.


كُتِب بواسطة: Ghanaian folktale
رسمة بواسطة: Wiehan de Jager
بترجمة: Sitwe Benson Mkandawire
لغة: الشيشيوا
مستوى: المستوى 3
المصدر: Anansi and Wisdom از القصص الأفريقية القصيرة
رخصة المشاع الإبداعي
تحت مجوز المشاع الإبداعي نَسب المُصنَّف 3.0 دولي کریتز کامنز به نشر رسید.
خيارات
العودة لقائمة القصص تحميل بصيغة PDF