Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Cuti Kwa Ambuya De vacaciones con la abuela

Texto Violet Otieno

Ilustraciones Catherine Groenewald

Translated by Bether Mwale Moyo

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 4

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Odongo ndi Apiyo anali kukhala mu tauni ndi atate awo. Amakondwelela masiku acuti. Sikuti Kamba kakuti masukulu anatsekela, koma cifukwa amapita kwa agogo awo. Agogo awo anali kukhala m’mudzi wogwila nsomba pafupi ndi nyanja yaiukulu.

Odongo y Apiyo vivían en la ciudad con su padre. Esperaban con ansias sus vacaciones. No sólo porque cerraban la escuela, sino porque iban a visitar a su abuela. Ella vivía en una aldea de pescadores cerca de un gran lago.


Odongo ndi Apiyo anali okondwela cifukwa inali nthawi yokayendelanso agogo awo. Usiku wa ulendo usanacitike, analongelato katundu kukonzekela ulendo wautali kupita kumudzi. Usiku uyu, anawa, sanagone ndipo anacezela kulankhula usiku wonse pa za cuti.

Odongo y Apiyo estaban emocionados con la idea de visitar de nuevo a su abuela. La noche antes del viaje, empacaron sus cosas y dejaron todo listo para irse a la aldea. No pudieron dormir y se quedaron toda la noche hablando sobre sus vacaciones.


M’mamawa kutaca, ulendo unapangika wopita kumudzi mgalimoto ya atate awo. Anayenda kupitilila maphili, nyama zamuthengo ndi minda ikulu-ikulu kwambili. Ana awa, anawelenga magalimoto munjila ndipo anayimba nyimbo.

Temprano a la mañana siguiente, salieron de viaje a la aldea en el auto de su padre. Pasaron por las montañas y vieron animales salvajes y plantaciones de té. Contaron autos y cantaron canciones.


Patapita nthawi, ana awa analema ndipo anagona.

Al poco tiempo, se cansaron y se quedaron dormidos.


Pamene anafika mu mudzi, atate awo anautsa Odongo ndi Apiyo. Anapeza Nyar-Kanyada, ambuya awo aligone pa mpasa munsi mwa mutengo. Nyar-Kanyada muciluo, atanthauza kuti “mwana wamkazi wa a Kanyada.” Ambuya awo anali muzimai wampamvu, ndipo wokongola kwambili.

El padre despertó a Odongo y Apiyo cuando llegaron a la aldea. Se encontraron a su abuela, Nyar-Kanyada, descansando con una manta debajo de un árbol. Nyar-Kanyada significa “hija de la gente de Kanyada” en el idioma Luo. La abuela era una mujer fuerte y hermosa.


Ambuya anakondwela kwambili ndipo anavina vina, nayimba nyimbo zacisangalalo. Azukulu nawo anakondwela kwambili, ndipo anapasa ambuya awo mpaso zomwe anawabwelesela. “Yambililani kusegula yanga mpaso,” anati Odongo. “Yambililani yanga,” anati Apiyo.

Nyar-Kanyada les dio la bienvenida a su casa, bailando y cantando de alegría. Sus nietos estaban ansiosos por entregarle los regalos que le trajeron de la ciudad. “Abre mi regalo primero,” dijo Odongo. “¡No, mi regalo primero!” dijo Apiyo.


Pomwe anasegula mpaso, Ambuya awo anawadalisa azukulu awo monga mwa mwambo.

Después de abrir los regalos, Nyar-Kanyada le dio la bendición tradicional a sus nietos.


Ndipo Odongo na Apiyo anayenda panja nayamba kupilikisa ma bulaula na mbalame.

Después, Odongo y Apiyo salieron a jugar. Persiguieron mariposas y aves.


Ana awa, anakwela mitengo ndipo anasewela m’madzi amnyanja.

Escalaron árboles y chapotearon en el lago.


Pamene kunada, ana anabwelela kunyumba kukadya cakudya ca madzulo. Koma akalibe kutsiliza kudya, anayamba kumva tulo!

Cuando oscureció, volvieron a la casa a cenar. ¡Se estaban quedando dormidos antes de terminar de comer!


M’mawa mwake, atate awo a Odongo ndi Apiyo anabwelela ku tauni ndikuwasiya ndi ambuya awo Nyar-Kanyada.

Al día siguiente, el padre de los niños se fue de vuelta a la ciudad y los dejó con Nyar-Kanyada.


Odongo ndi Apiyo anathandiza ambuya awo nchito za panyumba. Ana awa anatunga madzi ndi kusakila nkhuni. Anatola mazila ankhuku ndi kuthyola ndiyo m’dimba.

Odongo y Apiyo ayudaron a su abuela con las tareas del hogar. Fueron a buscar agua y leña. Recolectaron los huevos de las gallinas y recolectaron verduras de la huerta.


Ambuya awo anapunzisa adzukulu awo kuphika nsima, nsomba, ndi ndiyo zina zakumudzi.

Nyar-Kanyada le enseñó a sus nietos a hacer ugali para comer con estofado. Les enseñó a hacer arroz con coco para comerlo con pescado asado.


Tsiku lina, Odongo anapita kukadyetsela ng’ombe. Ng’ombe zina zinalowa m’munda mwa anthu ena. Mlimiyu anakalipila Odongo kwambili. Anaopseza kuti adzasunga pakudya mbewu zake. Patapita tsikulo, munyamata anatsimikidza kuti ng’ombe zisakhalenso mumabvuto.

Una mañana, Odongo llevó a las vacas de su abuela a pastar. Pero las vacas entraron en la granja de un vecino. El vecino se enojó con Odongo. Lo amenazó con quedarse con las vacas por haberse comido sus cultivos. Después de ese día, Odongo se aseguró que las vacas no se volvieran a meter en problemas.


Tsiku linanso, ana anapitaa ku musika ndi ambuya awo. Anali ndi stolo yogulitsamo ndiyo za m’munda, shuga ndi sopo. Apiyo anali kukonda kuuza anthu ogula mitengo ya zinthu. Odongo anali kukonda kulongeza zinthu zimene anthu anali kugula.

Otro día, los niños fueron al mercado con Nyar-Kanyada. Ella tenía un puesto para vender vegetales, azúcar y jabón. A Apiyo le gustaba decirle a los clientes cuánto costaban los productos. Odongo empacaba los productos para los clientes.


Pakuthela kwa tsiku anali kumwa tiyi ya chai pamodzi. Anathandiza ambuya awo kuwelenga ndalama zimene analinazo.

Al final del día, tomaban té juntos. Le ayudaban a su abuela a contar cuánto dinero había ganado.


Koma mosacedwa cuti cinali kutha ndipo ana amafunika kubwelela ku tauni. Ambuya anapatsa Odongo kapu ndipo anapatsa Apiyo juzi. Ambuya analonga cakudya capaulendo.

Pero las vacaciones se terminaron muy rápido y los niños tuvieron que regresar a la ciudad. Nyar-Kanyada le regaló una gorra a Odongo y un chaleco a Apiyo. Luego les empacó comida para su viaje de vuelta a casa.


Odongo ndi Apiyo sibanafune kubwelela ku tauni. Anapempha ambuya awo kuti apite nawo ku tauni. Koma ambuya anamwetula nati, “Ndine okalamba kwambili ndipo sindingahkale mu tauni. Ndizayamba kukuyembekeza kubwelanso kwanu kuno kumudzi.”

Cuando su padre vino a recogerlos, no querían irse. Los niños le suplicaron a Nyar-Kanyada que se fuera con ellos a la ciudad. Ella sonrió y les dijo: “Estoy muy vieja para la ciudad. Estaré esperándolos cuando vuelvan a mi aldea otra vez.”


Odongo ndi Apiyo anakumbatilana nao ambuya awo nalayilana.

Odongo y Apiyo le dieron un abrazo muy apretado y le dijeron adiós.


Pamene Odongo nda Apiyo anabwelela kusukulu, anauza anzao za umoyo wakumudzi. Ana ena anadziwa kuti umoyo wa mtauni ndi wabwino. Ena anakonda umoyo wakumudzi. Koma ambili a iwo, onse ananena kuti ambuya a Odongo ndi Apiyo anali abwino mtima!

Cuando Odongo y Apiyo volvieron a la escuela, le hablaron a sus amigos acerca de la vida en la aldea. Algunos niños opinaron que la vida en la ciudad era buena. Otros opinaron que la aldea era mejor. ¡Pero lo más importante es que todos opinaron que Odongo y Apiyo tenían una abuela maravillosa!


Texto: Violet Otieno
Ilustraciones: Catherine Groenewald
Translated by: Bether Mwale Moyo
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 4
Fuente: Holidays with grandmother del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 4.0 Internacional.
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF