Descargar PDF
Regresar a lista de cuentos

Simbegwire Simbegwire

Texto Rukia Nantale

Ilustraciones Benjamin Mitchley

Translated by Fredrick Mapulanga

Lectura en voz alta Christine Mwanza

Lengua chinyanja

Nivel Nivel 5

Contar el cuento completo El audio no está disponible actualmente.


Pamene amai a Simbegwire anamwalila, anakhala wacisoni kwambili. Abambo a Simbegwire adacita zothekela zonse kusamalila mwana wawo wamkazi. Pang’ono-pang’ono, adaphunzilanso kusangalalanso, popanda amai a Simbegwire. M’mawa mulimonse amakhala ndikulankhula za tsiku la mawa. Madzulo mulimonse ankadyela pamodzi cakudya camadzulo. Atatsuka mbale, bambo wa Simbegwire anamuthandiza ntchito yasukulu yakunyumba.

Cuando la madre de Simbegwire murió, ella estaba muy triste. El padre de Simbegwire hizo lo mejor que pudo para cuidar de su hija. Lentamente, aprendieron a ser felices de nuevo, sin la madre de Simbegwire. Cada mañana, se sentaban y hablaban sobre el siguiente día. Cada tarde, hacían la cena juntos. Luego, lavaban los platos y el padre de Simbegwire la ayudaba con sus tareas.


Tsiku lina, abambo a Simbegwire adafika kunyumba mocedwa kuposa masiku onse. “Kodi mwana wanga uli kuti?” adayitana. Simbegwire anathamangila kwa abambo ake. Anayima pomwe anawona kuti anagwilila dzanja la mkazi. “Ndikufuna iwe ukumane ndi munthu wapadela, mwana wanga. Uyu ndi Anita,” anatelo akumwetulila.

Un día, el padre de Simbegwire llegó a casa más tarde de lo usual. “¿Dónde estás mi niña?” él preguntó. Simbegwire corrió hacia su padre, y quedó inmóvil cuando vio que él estaba tomado de la mano con una mujer. “Quiero que conozcas a alguien muy especial, mi niña. Ella es Anita,” dijo sonriendo.


“Moni Simbegwire, abambo ako andiuza zambili za iwe,” anatelo Anita. Koma sanamwetulile kapena kugwilila dzanja la mtsikanayo. Abambo a Simbegwire anali okondwa komanso osangalala. Anakambilana za atatuwa kukhala pamodzi, komanso momwe moyo wawo ungakhalile bwino. “Mwana wanga, ndikhulupilila kuti wavomela Anita kukhala amai ako,” anatelo.

“Hola Simbegwire, tu padre me ha contado mucho sobre ti,” dijo Anita. Pero no le sonrió ni tomó de la mano. El padre de Simbegwire estaba feliz y emocionado. Él habló sobre los tres viviendo juntos, y cuán bueno eso sería. “Mi niña, espero que aceptes a Anita como tu madre,” él dijo.


Moyo wa Simbegwire unasintha. Sanalinso ndi nthawi yoceza ndi bambo ake m’mawa. Anita anam’patsa ntchito zambili zapanyumba kotelo kuti anali wotopa kwambili kugwila ntchito yake yakusukulu m’madzulo. Anangopita kukagona atadya cakudya camadzulo. Comwe cinangomutonthoza cinali bulangete wokongola womwe amai ake anampatsa. Abambo a Simbegwire sanadzindikile konse kuti mwana wawo anali wosasangalala.

La vida de Simbegwire cambió. Ya no tenía tiempo para sentarse con su padre por las mañanas. Anita le dio muchas tareas domésticas que la agotaban demasiado para hacer sus tareas escolares por las tardes. Ella se iba directo a su cama después de cenar. Su único consuelo era su manta colorida que su madre le regaló. El padre de Simbegwire no parecía notar que su hija estaba triste.


Patapita miyezi yaing’ono, abambo a Simbegwire anafotokoza kuti adzacokapo pa nyumba kwakanthawi. “Ndiyenela kupita kuntchito yanga,” adatelo. “Koma ndikudziwa mudzasamalilana.” Nkhope ya Simbegwire idagwa, koma abambo ake sanazindikile konse. Anita sananene ciliconse. Sanasangalale nayenso.

Después de varios meses, el padre de Simbegwire les dijo que él estaría fuera de casa por un tiempo. “Tengo que viajar por mi trabajo,” él dijo. “Pero sé que ustedes se cuidarán la una a la otra.” Simbegwire puso cara de decepción, pero su padre no la notó. Anita no dijo nada. Ella tampoco estaba contenta.


Zinthu zinafika poipa kwa Simbegwire. Ngati sanamalize ntchito zake, kapena kumadandaula, Anita amamumenya. Ndipo pacakudya camadzulo, maiyo amadya cakudya cambili, nasiyila Simbegwire zidutswa zocepa cabe. Usiku uliwonse Simbegwire amalila yekha kugona, kukumbatila bulangete wa amai ake.

Las cosas se pusieron peores para Simbegwire. Si no terminaba sus tareas de la casa, o si se quejaba, Anita la golpeaba. Y a la hora de la cena, la mujer se comía la mayor parte de la comida, dejando sólo las sobras para Simbegwire. Cada noche, Simbegwire lloraba hasta quedarse dormida, abrazando la manta de su madre.


Tsiku lina m’mawa, Simbegwire anacedwa kuuka. “Iwe mwana waulesi!” Anita anafuula. Anamcotsa Simbegwire pabedi. Bulangete wamtengo wapatali anagwidwa ndi msomali, ndipo unang’ambika pakati.

Una mañana, Simbegwire se atrasó en levantarse. “¡Qué niña más floja!” Anita le gritó. Ella la tiró fuera de la cama. La manta tan preciada de Simbegwire que había quedado enganchada en un clavo, se rasgó en dos.


Simbegwire anakhumudwa kwambili. Anaganiza zothawa kucoka panyumba. Anatenga zidutswa za bulangete wa amai ake, nanyamula cakudya, natuluka mnyumbamo. Anatsatila njila yomwe abambo ake anapitila.

Simbegwire estaba muy enfadada. Ella decidió irse de su casa. Tomó los pedazos de la manta de su madre, empacó un poco de comida y se fue de casa. Siguió el mismo camino que su padre había tomado.


Pofika madzulo, anakwela mtengo wautali pafupi ndi mtsinje ndipo anadzipangila pogona panthambi. Pomwe anagona, anayimba: Maama, maama, maama, munandisiya. Munandisiya osabwelanso. Atate sakundikondanso. Amai, mudzabwela liti? Munandisiya.”

Cuando atardeció, Simbegwire se trepó a un árbol muy alto que estaba cerca de un riachuelo e hizo una cama en sus ramas. Mientras se quedaba dormida, ella cantaba: “Maamá, maamá, maamá, me abandonaste. Me abandonaste y nunca regresaste. Mi padre ya no me ama. Madre, ¿cuándo regresarás? Me abandonaste.”


M’mawa mwake, Simbegwire anayimbanso nyimboyo. Pomwe azimaimai anabwela kudzachapa zovala zawo pamtsinje, anamva nyimbo yacisoni ikucokela mumtengo wautali. Amaganiza kuti ndi mphepo yomwe imawaza masamba, ndikupitilila ndi ntchito yawo. Koma m’modzi mwa azimaiwo anamvetsela mosamalitsa ku nyimboyi.

A la mañana siguiente, Simbegwire cantó una vez más. Cuando unas mujeres vinieron a lavar sus ropas en el riachuelo, escucharon la triste canción que venía de lo alto del árbol. Pensaron que sólo era el viento moviendo las hojas, y siguieron con su trabajo. Pero una de las mujeres le puso más atención a la canción.


Mai uyu anayang’ana m’mtengo. Ataona mtsikanayo ndi zidutswa za bulangete wokongola, aafuula, “Simbegwire, mwana wa mcimwene wanga!” Amai enawo anasiya kutsuka ndikuthandizila Simbegwire kutsika m’mtengo. Azakhali ake anakumbatila kamtsikanaka ndikuyesetsa kumutonthoza.

Esta mujer miró hacia arriba del árbol. Cuando vio a la niña con su manta en pedazos, gritó, “¡Simbegwire, la hija de mi hermano!” Las otras mujeres dejaron de lavar y ayudaron a Simbegwire a bajar del árbol. Su tía la abrazó y trató de consolarla.


Azakhali ake a Simbegwire adapita ndi mwana kunyumba kwake. Anapatsa Simbegwire cakudya cothuma, ndikumugoneka pabedi ndi bulangete wa amai ake. Usiku womwewo, Simbegwire analila pamene anali kugona. Koma inali misozi yampumulo. Anadziwa kuti azakhali ake azamusamalila.

La tía de Simbegwire la llevó a su casa. Le dio de comer, y la acomodó en la cama con la manta de su madre. Esa noche, Simbegwire lloraba mientras se quedaba dormida. Pero eran lágrimas de alegría. Sabía que su tía cuidaría de ella.


Pamene abambo a Simbegwire atabwelelako, anapeza cipinda cake cilibe kanthu. “Cinacitika ndi ciani, Anita?” anafunsa ndi mtima wokhumudwa. Maiyo analongosola kuti Simbegwire anathawa. “Ndidafuna kuti iye andilemekeze,” anatelo. “Koma mwina ndinali okhwimitsa zinthu.” Abambo a Simbegwire anacoka mnyumbamo ndi kulowela ca kumtsinje. Adapitilizabe kupita kumudzi kwa mlongo wake kuti akafunse ngati anamuonako Simbegwire.

Cuando el padre de Simbegwire regresó a casa, encontró su habitación vacía. “¿Qué ocurrió, Anita?” él preguntó con gran tristeza. La mujer le dijo que Simbegwire había huido de casa. “Quería que me respetara,” ella dijo. “Pero quizás fui muy estricta.” El padre de Simbegwire salió de la casa y caminó con dirección hacia el riachuelo. Siguió caminando hasta la villa de su hermana para preguntarle por Simbegwire.


Simbegwire anali kusewela ndi azisuweni ake ataona bambo wake kutali. Anacita mantha kuti mwina adzakwiya, motelo anathamangila mnyumba kukabisala. Koma abambo ake anapita kwa iye nati, “Simbegwire, wadzipezela wekha mai wako wabwino mai. Yemwe akukonda ndikukumvetsetsa. Ndikunyadila ndipo ndikukonda.” Anagwilizana kuti Simbegwire azikhala ndi azakhali ake kulingana ndi momwe angafunile.

Simbegwire estaba jugando con sus primos cuando vio a su padre de lejos. Ella tenía miedo de que estuviera enfadado, así que corrió a esconderse. Pero su padre la siguió y le dijo, “Simbegwire, has encontrado a la madre perfecta para ti. Una madre que te ama y te entiende. Estoy orgulloso de ti y te amo.” Los dos estaban de acuerdo en que Simbegwire podía quedarse con su tía el tiempo que quisiera.


Abambo ake amamuyendela tsiku lililonse. Pambuyo pake, anabwela ndi Anita. Anatambasulila dzanja lake kwa Simbegwire. “Pepani, ndinalakwitsa,” analila. “Kodi ungandilole kuyesanso?” Simbegwire anayang’ana abambo ake ndi nkhope yawo ya nkhawa. Kenako anayenda pang’ono pang’ono cakutsogolo ndikukumbatila Anita.

Su padre la visitaba todos los días. Con el paso del tiempo, él llevó a Anita. Ella tomó la mando de Simbegwire. “Lo siento mucho pequeñita, me equivoqué,” le dijo. “¿Me darías otra oportunidad?” Simbegwire volteó a mirar a su padre, quien lucía preocupado. Entonces, ella se acercó a Anita lentamente y la abrazó.


Sabata yotsatila, Anita adayitanitsa Simbegwire, ndi abale ake ndi azakhali ake, kunyumba kuti akadye. Ndi phwando labwino bwanji! Anita anakonza zakudya zonse zomwe Simbegwire amakonda, ndipo aliyense anadya mpaka atakhuta. Kenako ana anasewela pomwe akulu amalankhula. Simbegwire anali wosangalala komanso wolimba mtima. Anaganiza kuti posachedwa, abwelela kunyumba kukakhala ndi abambo ndi amai ake omupeza.

A la semana siguiente, Anita invitó a Simbegwire, a sus primos y a su tía, a cenar en su casa. ¡Qué gran festín! Anita cocinó todas las comidas favoritas de Simbegwire, y todos comieron hasta quedar satisfechos. Luego, los niños jugaron y los adultos charlaron. Simbegwire se sentía feliz y valiente. Ella había decidido que pronto, muy pronto, regresaría a casa para vivir con su padre y su madrastra.


Texto: Rukia Nantale
Ilustraciones: Benjamin Mitchley
Translated by: Fredrick Mapulanga
Lectura en voz alta: Christine Mwanza
Lengua: chinyanja
Nivel: Nivel 5
Fuente: Simbegwire del African Storybook
Licencia Creative Commons
Esta obra está bajo una Creative Commons Atribución 3.0 Internacional.
Leer más cuentos nivel 5:
Opciones
Regresar a lista de cuentos Descargar PDF