Téléchargement PDF
Retour à la liste des contes

Simbegwire Simbegwire

Écrit par Rukia Nantale

Illustré par Benjamin Mitchley

Traduit par Fredrick Mapulanga

Lu par Christine Mwanza

Langue chewa

Niveau Niveau 5

Lire l’histoire en entier L’enregistrement audio de cette histoire est actuellement indisponible.


Pamene amai a Simbegwire anamwalila, anakhala wacisoni kwambili. Abambo a Simbegwire adacita zothekela zonse kusamalila mwana wawo wamkazi. Pang’ono-pang’ono, adaphunzilanso kusangalalanso, popanda amai a Simbegwire. M’mawa mulimonse amakhala ndikulankhula za tsiku la mawa. Madzulo mulimonse ankadyela pamodzi cakudya camadzulo. Atatsuka mbale, bambo wa Simbegwire anamuthandiza ntchito yasukulu yakunyumba.

Quand la mère de Simbegwire décéda, Simbegwire fut très triste. Son père essaya de son mieux de prendre soin de sa fille. Lentement, ils apprirent comment se sentir heureux de nouveau, sans la mère de Simbegwire. Chaque matin, ils s’asseyaient et discutaient de la journée à venir. Chaque soir, ils cuisinaient le souper ensemble. Après avoir lavé la vaisselle, le père de Simbegwire l’aidait avec ses devoirs.


Tsiku lina, abambo a Simbegwire adafika kunyumba mocedwa kuposa masiku onse. “Kodi mwana wanga uli kuti?” adayitana. Simbegwire anathamangila kwa abambo ake. Anayima pomwe anawona kuti anagwilila dzanja la mkazi. “Ndikufuna iwe ukumane ndi munthu wapadela, mwana wanga. Uyu ndi Anita,” anatelo akumwetulila.

Un jour, le père de Simbegwire retourna chez eux plus tard que d’habitude. « Où es-tu mon enfant ? » demanda-t-il. Simbegwire se précipita vers son père. Elle s’arrêta en chemin quand elle vit qu’il tenait la main d’une femme. « Je veux te présenter quelqu’un de spécial, mon enfant. Voici Anita, » dit-il en souriant.


“Moni Simbegwire, abambo ako andiuza zambili za iwe,” anatelo Anita. Koma sanamwetulile kapena kugwilila dzanja la mtsikanayo. Abambo a Simbegwire anali okondwa komanso osangalala. Anakambilana za atatuwa kukhala pamodzi, komanso momwe moyo wawo ungakhalile bwino. “Mwana wanga, ndikhulupilila kuti wavomela Anita kukhala amai ako,” anatelo.

« Bonjour Simbegwire, ton père m’a beaucoup parlé de toi, » dit Anita. Mais elle ne sourit pas et ne serra pas la main de la fille. Le père de Simbegwire était content et excité. Il dit qu’ils allaient vivre ensemble tous les trois et qu’ils auraient une bonne vie. « Mon enfant, j’espère que tu accepteras Anita comme ta mère, » dit-il.


Moyo wa Simbegwire unasintha. Sanalinso ndi nthawi yoceza ndi bambo ake m’mawa. Anita anam’patsa ntchito zambili zapanyumba kotelo kuti anali wotopa kwambili kugwila ntchito yake yakusukulu m’madzulo. Anangopita kukagona atadya cakudya camadzulo. Comwe cinangomutonthoza cinali bulangete wokongola womwe amai ake anampatsa. Abambo a Simbegwire sanadzindikile konse kuti mwana wawo anali wosasangalala.

La vie de Simbegwire changea. Elle n’avait plus le temps de s’asseoir avec son père le matin. Anita lui donnait tellement de tâches ménagères qu’elle était trop fatiguée pour faire ses devoirs le soir. Elle allait directement se coucher après le souper. Son seul confort était la couverture colorée que sa mère lui avait faite. Le père de Simbegwire ne semblait pas remarquer que sa fille était malheureuse.


Patapita miyezi yaing’ono, abambo a Simbegwire anafotokoza kuti adzacokapo pa nyumba kwakanthawi. “Ndiyenela kupita kuntchito yanga,” adatelo. “Koma ndikudziwa mudzasamalilana.” Nkhope ya Simbegwire idagwa, koma abambo ake sanazindikile konse. Anita sananene ciliconse. Sanasangalale nayenso.

Après quelques mois, le père de Simbegwire annonça qu’il serait parti pour un certain temps. « Je dois voyager pour mon travail, » dit-il. « Mais je sais que vous allez vous occuper l’une de l’autre. » Le visage de Simbegwire s’allongea, mais son père ne le remarqua pas. Anita ne dit rien. Elle n’était pas contente non plus.


Zinthu zinafika poipa kwa Simbegwire. Ngati sanamalize ntchito zake, kapena kumadandaula, Anita amamumenya. Ndipo pacakudya camadzulo, maiyo amadya cakudya cambili, nasiyila Simbegwire zidutswa zocepa cabe. Usiku uliwonse Simbegwire amalila yekha kugona, kukumbatila bulangete wa amai ake.

Les choses s’empirèrent pour Simbegwire. Si elle ne terminait pas ses tâches, ou si elle se plaignait, Anita la frappait. Et pendant le souper, la femme mangeait la plupart de la nourriture, laissant Simbegwire avec peu de restes. Chaque nuit Simbegwire s’endormait en pleurant, embrassant la couverture de sa mère.


Tsiku lina m’mawa, Simbegwire anacedwa kuuka. “Iwe mwana waulesi!” Anita anafuula. Anamcotsa Simbegwire pabedi. Bulangete wamtengo wapatali anagwidwa ndi msomali, ndipo unang’ambika pakati.

Un matin, Simbegwire se leva en retard. « Paresseuse ! » cria Anita. Elle tira Simbegwire de son lit. La couverture précieuse resta accrochée sur un clou et se déchira en deux.


Simbegwire anakhumudwa kwambili. Anaganiza zothawa kucoka panyumba. Anatenga zidutswa za bulangete wa amai ake, nanyamula cakudya, natuluka mnyumbamo. Anatsatila njila yomwe abambo ake anapitila.

Simbegwire était très bouleversée. Elle décida de se sauver de chez elle. Elle prit les morceaux de couverture de sa mère, emporta de la nourriture et quitta la maison. Elle suivit le chemin que son père avait pris.


Pofika madzulo, anakwela mtengo wautali pafupi ndi mtsinje ndipo anadzipangila pogona panthambi. Pomwe anagona, anayimba: Maama, maama, maama, munandisiya. Munandisiya osabwelanso. Atate sakundikondanso. Amai, mudzabwela liti? Munandisiya.”

Quand le soir arriva, elle grimpa dans un arbre près d’un ruisseau et se fit un lit dans les branches. En s’endormant, elle chanta, « Maman, maman, maman, tu m’as quittée. Tu m’as quittée et tu n’es jamais revenue. Papa ne m’aime plus. Maman, quand reviens-tu ? Tu m’as quittée. »


M’mawa mwake, Simbegwire anayimbanso nyimboyo. Pomwe azimaimai anabwela kudzachapa zovala zawo pamtsinje, anamva nyimbo yacisoni ikucokela mumtengo wautali. Amaganiza kuti ndi mphepo yomwe imawaza masamba, ndikupitilila ndi ntchito yawo. Koma m’modzi mwa azimaiwo anamvetsela mosamalitsa ku nyimboyi.

Le lendemain matin, Simbegwire chanta encore la chanson. Quand les femmes arrivèrent au ruisseau pour laver leur linge, elles entendirent la chanson triste qui venait du grand arbre. Elles pensaient que c’était seulement le bruissement des feuilles et continuèrent leur travail. Mais une des femmes écouta la chanson attentivement.


Mai uyu anayang’ana m’mtengo. Ataona mtsikanayo ndi zidutswa za bulangete wokongola, aafuula, “Simbegwire, mwana wa mcimwene wanga!” Amai enawo anasiya kutsuka ndikuthandizila Simbegwire kutsika m’mtengo. Azakhali ake anakumbatila kamtsikanaka ndikuyesetsa kumutonthoza.

Cette femme jeta un coup d’œil dans l’arbre. Quand elle vit la fille et les morceaux de couverture colorés, elle cria, « Simbegwire, l’enfant de mon frère ! » Les autres femmes s’arrêtèrent de laver et aidèrent Simbegwire à descendre de l’arbre. Sa tante l’embrassa et essaya de la réconforter.


Azakhali ake a Simbegwire adapita ndi mwana kunyumba kwake. Anapatsa Simbegwire cakudya cothuma, ndikumugoneka pabedi ndi bulangete wa amai ake. Usiku womwewo, Simbegwire analila pamene anali kugona. Koma inali misozi yampumulo. Anadziwa kuti azakhali ake azamusamalila.

La tante de Simbegwire l’emmena chez elle. Elle donna à Simbegwire un repas chaud et la borda dans son lit avec la couverture de sa mère. Ce soir-là, Simbegwire s’endormit en pleurant. Mais ses larmes étaient des larmes de joie. Elle savait que sa tante prendrait soin d’elle.


Pamene abambo a Simbegwire atabwelelako, anapeza cipinda cake cilibe kanthu. “Cinacitika ndi ciani, Anita?” anafunsa ndi mtima wokhumudwa. Maiyo analongosola kuti Simbegwire anathawa. “Ndidafuna kuti iye andilemekeze,” anatelo. “Koma mwina ndinali okhwimitsa zinthu.” Abambo a Simbegwire anacoka mnyumbamo ndi kulowela ca kumtsinje. Adapitilizabe kupita kumudzi kwa mlongo wake kuti akafunse ngati anamuonako Simbegwire.

Quand le père de Simbegwire rentra chez lui, il trouva la chambre de sa fille vide. « Qu’est-ce qui est arrivé, Anita ? » demanda-t-il, le cœur gros. La femme expliqua que Simbegwire s’était sauvée. « Je voulais qu’elle me respecte, » dit-elle. « Mais j’ai peut-être été trop sévère. » Le père de Simbegwire quitta la maison et se dirigea dans la direction du ruisseau. Il se rendit au village de sa sœur pour découvrir si elle avait vu Simbegwire.


Simbegwire anali kusewela ndi azisuweni ake ataona bambo wake kutali. Anacita mantha kuti mwina adzakwiya, motelo anathamangila mnyumba kukabisala. Koma abambo ake anapita kwa iye nati, “Simbegwire, wadzipezela wekha mai wako wabwino mai. Yemwe akukonda ndikukumvetsetsa. Ndikunyadila ndipo ndikukonda.” Anagwilizana kuti Simbegwire azikhala ndi azakhali ake kulingana ndi momwe angafunile.

Simbegwire jouait avec ses cousins quand elle vit son père de loin. Elle avait peur qu’il soit peut-être fâché, alors elle se précipita à l’intérieur de la maison pour se cacher. Mais son père vint la voir et lui dit, « Simbegwire, tu t’es trouvé une mère parfaite. Une mère qui t’aime et te comprend. Je suis fier de toi et je t’aime. » Ils se mirent d’accord que Simbegwire resterait avec sa tante aussi longtemps qu’elle le voudrait.


Abambo ake amamuyendela tsiku lililonse. Pambuyo pake, anabwela ndi Anita. Anatambasulila dzanja lake kwa Simbegwire. “Pepani, ndinalakwitsa,” analila. “Kodi ungandilole kuyesanso?” Simbegwire anayang’ana abambo ake ndi nkhope yawo ya nkhawa. Kenako anayenda pang’ono pang’ono cakutsogolo ndikukumbatila Anita.

Son père lui rendit visite chaque jour. Finalement, il vint avec Anita. Elle tendit la main vers celle de Simbegwire. « Je suis tellement désolée, petite, j’ai eu tort, » sansanglota-t-elle. « Me laisseras-tu essayer de nouveau ? » Simbegwire examina son père et son regard inquiet. Puis elle fit lentement un pas en avant et mit ses bras autour d’Anita.


Sabata yotsatila, Anita adayitanitsa Simbegwire, ndi abale ake ndi azakhali ake, kunyumba kuti akadye. Ndi phwando labwino bwanji! Anita anakonza zakudya zonse zomwe Simbegwire amakonda, ndipo aliyense anadya mpaka atakhuta. Kenako ana anasewela pomwe akulu amalankhula. Simbegwire anali wosangalala komanso wolimba mtima. Anaganiza kuti posachedwa, abwelela kunyumba kukakhala ndi abambo ndi amai ake omupeza.

La semaine suivante, Anita invita Simbegwire, ainsi que ses cousins et sa tante, chez elle pour un repas. Quel festin ! Anita prépara tous les plats favoris de Simbegwire et tous mangèrent jusqu’à temps qu’ils soient repus. Ensuite, les enfants jouèrent tandis que les adultes parlaient. Simbegwire se sentait contente et courageuse. Elle décida que bientôt, très bientôt, elle retournerait chez elle pour vivre avec son père et sa belle-mère.


Écrit par: Rukia Nantale
Illustré par: Benjamin Mitchley
Traduit par: Fredrick Mapulanga
Lu par: Christine Mwanza
Langue: chewa
Niveau: Niveau 5
Source: Simbegwire du Livre de contes africains
Licence de Creative Commons
Ce travail est autorisé sous une licence Creative Commons Attribution 3.0 non transposé.
Lire plus de contes de niveau 5 :
Options
Retour à la liste des contes Téléchargement PDF